Categories
NEHEMIYA

NEHEMIYA 11

Ena akhala mu Yerusalemu, ena m’midzi ina

1 Ndipo akulu a anthu anakhala muYerusalemu; anthu otsala omwe anachita maere, kuti libwere limodzi la magawo khumi likhale mu Yerusalemu, mzinda wopatulika, ndi asanu ndi anai akhumi m’mizinda ina.

2 Ndipo anthu anadalitsa amuna onse akudzinenera mwaufulu kuti adzakhala mu Yerusalemu.

3 Awa tsono ndi akulu a dziko okhala mu Yerusalemu; koma m’midzi ya Yuda yense anakhala pa cholowa chake m’midzi mwao, ndiwo Israele, ansembe, ndi Alevi, ndi antchito a m’kachisi, ndi ana a akapolo a Solomoni.

4 Ndipo mu Yerusalemu munakhala ena a ana a Yuda ndi ana a Benjamini. Mwa ana a Yuda: Ataya mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya, mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalalele, wa ana a Perezi;

5 ndi Maaseiya mwana wa Baruki, mwana wa Kolihoze, mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yoyaribu, mwana wa Zekariya, mwana wa Msiloni.

6 Ana onse a Perezi okhala mu Yerusalemu ndiwo ngwazi mazana anai mphambu makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi atatu.

7 Ndi ana a Benjamini ndi awa: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yoedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itiyele, mwana wa Yesaya.

8 Ndi wotsatana naye Gabai, Salai, mazana asanu ndi anai mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.

9 Ndi Yowele mwana wa Zikiri ndiye woyang’anira wao, ndi Yuda mwana wa Hasenuwa ndiye wothandizana naye, poyang’anira mzinda.

10 Mwa ansembe: Yedaya mwana wa Yoyaribu, Yakini,

11 Seraya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Meraiyoti, mwana wa Ahitubi mtsogoleri wa m’nyumba ya Mulungu;

12 ndi abale ao ochita ntchito ya m’nyumbayi ndiwo mazana asanu ndi atatu mphambu makumi awiri kudza awiri; ndi Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasuri, mwana wa Malikiya;

13 ndi abale ake akulu a nyumba za makolo awiri mphambu makumi anai kudza awiri, ndi Amasisai mwana wa Azarele, mwana wa Ahazai, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri;

14 ndi abale ao, ngwazi zamphamvu, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu; ndi woyang’anira wao ndiye Zabidiele mwana wa Hagedolimu.

15 Ndi mwa Alevi: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni;

16 ndi Sabetai, ndi Yozabadi, mwa akulu a Alevi, anayang’anira ntchito za pabwalo za nyumba ya Mulungu;

17 ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu, ndiye mkulu wakuyamba mayamiko, popemphera; ndi Bakibukiya wotsatana naye mwa abale ake, ndi Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.

18 Alevi onse m’mzinda wopatulikawo ndiwo mazana awiri mphambu makumi asanu ndi atatu kudza anai.

19 Ndi odikira: Akubu, Talimoni, ndi abale ao akulindira pazipata, ndiwo zana limodzi mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.

20 Ndi Aisraele otsala ndiwo ansembe ndi Alevi, anakhala m’midzi yonse ya Yuda, yense m’cholowa chake.

21 Koma antchito a m’kachisi anakhala mu Ofele, ndi Ziha, ndi Gisipa anali oyang’anira antchito a m’kachisi.

22 Ndipo woyang’anira wa Alevi mu Yerusalemu ndiye Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika; mwa ana a Asafu oimbira ena anayang’anira ntchito ya m’nyumba ya Mulungu.

23 Pakuti mfumu inalamulira za iwowa, naikira oimbira chowathandiza, yense chake pa tsiku lake.

24 Ndi Petahiya mwana wa Mesezabele, wa ana a Zera, mwana wa Yuda, anatumikira mfumu pa milandu yonse ya anthuwo.

25 Ndi ana ena a Yuda anakhala m’midzi ya kuminda yao, mu Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ndi mu Diboni ndi midzi yake, ndi mu Yekabizeele ndi midzi yake,

26 ndi mu Yesuwa, ndi mu Molada, ndi Betepeleti,

27 ndi mu Hazara-Suwala, ndi mu Beereseba ndi midzi yake,

28 ndi mu Zikilagi, ndi mu Mekona ndi midzi yake,

29 ndi mu Enirimoni, ndi mu Zora, ndi mu Yaramuti,

30 Zanowa, Adulamu ndi midzi yao, Lakisi ndi minda yake, Azeka ndi midzi yake. Ndipo anamanga misasa kuyambira ku Beereseba mpaka chigwa cha Hinomu.

31 Ana a Benjamini omwe, kuyambira ku Geba pa Mikimasi, ndi Aya, ndi pa Betele ndi midzi yake,

32 pa Anatoti, Nobi, Ananiya,

33 Hazori, Rama, Gitaimu,

34 Hadidi, Zeboimu, Nebalati,

35 Lodi, ndi Ono, chigwa cha amisiri.

36 Ndi magawo a Levi anakhala ena ku Yuda, ndi ena ku Benjamini.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NEH/11-f3c4f10c7ab83f701f0e3e896f785769.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *