Pangano lokhazikika pakati pa anthu ndi Mulungu
1 Okhomera chizindikiro tsono ndiwo Nehemiya, Tirisata mwana wa Hakaliya, ndi Zedekiya,
2 Seraya, Azariya, Yeremiya,
3 Pasuri, Amariya, Malikiya,
4 Hatusi, Sebaniya, Maluki,
5 Harimu, Meremoti, Obadiya,
6 Daniele, Ginetoni, Baruki,
7 Mesulamu, Abiya, Miyamini,
8 Maaziya, Biligai, Semaya, ndiwo ansembe.
9 Ndi Alevi ndiwo Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa ana a Henadadi, Kadimiyele;
10 ndi abale ao: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
11 Mika, Rehobu, Hasabiya,
12 Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
13 Hodiya, Bani, Beninu.
14 Akulu a anthu: Parosi, Pahatimowabu, Elamu, Zatu, Bani,
15 Buni, Azigadi, Bebai,
16 Adoniya, Bigivai, Adini,
17 Atere, Hezekiya, Azuri,
18 Hodiya, Hasumu, Bezai,
19 Harifi, Anatoti, Nebai,
20 Magapiyasi, Mesulamu, Heziri,
21 Mesezabele, Zadoki, Yaduwa,
22 Pelatiya, Hanani, Anaya,
23 Hoseya, Hananiya, Hasubu,
24 Halohesi, Piliha, Sobeki,
25 Rehumu, Hasabuna, Maaseiya,
26 ndi Ahiya, Hanani, Anani,
27 Maluki, Harimu, Baana.
28 Ndi anthu otsala, ansembe, Alevi, odikira, oimbira, antchito a m’kachisi, ndi onse anadzisiyanitsawo pa mitundu ya anthu a m’dziko kutsata chilamulo cha Mulungu, akazi ao, ana ao aamuna ndi aakazi, yense wodziwa ndi wozindikira,
29 amenewa anaumirira abale ao, omveka ao, nalowa m’temberero ndi lumbiro, kuti adzayenda m’chilamulo cha Mulungu anachipereka Mose mtumiki wa Mulungu, ndi kuti adzasunga ndi kuchita zonse atilamulira Yehova Ambuye wathu, ndi maweruzo ake, ndi malemba ake;
30 ndi kuti sitidzapereka ana athu aakazi kwa mitundu ya anthu a m’dziko, kapena kutengera ana athu aamuna ana ao aakazi;
31 ndipo mitundu ya anthu a m’dziko akabwera nao malonda, ngakhale tirigu, tsiku laSabata, kutsata malonda, sitidzagulana nao pa tsiku la Sabata, kapena tsiku lina lopatulika, ndi kuti tidzaleka chaka chachisanu ndi chiwiri ndi mangawa ali onse.
32 Tinadziikiranso malamulo, kuti tizipereka chaka ndi chaka limodzi la magawo atatu a sekeli kuntchito ya nyumba ya Mulungu wathu;
33 kulipereka mkate woonekera, ndi nsembe yaufa yosaleka, ndi nsembe yopsereza yosaleka, ya masabata, ya pokhala miyezi, kuliperekera nyengo zoikika ndi zopatulikira, ndi nsembe za zolakwa za kutetezera Israele zoipa, ndi ntchito zonse za nyumba ya Mulungu wathu.
34 Ndipo tinalota maere, ansembe, Alevi, ndi anthu, a chopereka cha nkhuni, kubwera nazo kunyumba ya Mulungu wathu, monga mwa nyumba za makolo athu, pa nyengo zoikika chaka ndi chaka, kuzisonkha paguwa la nsembe la Yehova Mulungu wathu, monga mulembedwa m’chilamulo;
35 ndi kubwera nazo zipatso zoyamba za nthaka, ndi zoyamba za zipatso zonse za mtengo uliwonse chaka ndi chaka, ku nyumba ya Yehova;
36 ndi ana athu oyamba kubadwa, ndi oyamba kubadwa a nyama zathu, monga mulembedwa m’chilamulo, ndi oyamba a ng’ombe zathu, ndi nkhosa zathu, kubwera nazo kunyumba ya Mulungu wathu kwa ansembe akutumikira m’nyumba ya Mulungu wathu;
37 ndi kuti tidzabwera nazo za mtanda wa mkate wathu woyamba, ndi nsembe zathu zokwera, ndi zipatso za mtengo uliwonse, vinyo, ndi mafuta, kwa ansembe, kuzipinda za nyumba ya Mulungu wathu; ndi limodzi la magawo khumi la nthaka yathu kwa Alevi; pakuti Alevi amene amalandira limodzilimodzi la magawo khumi m’midzi yonse yolima ife.
38 Ndipo wansembe mwana wa Aroni azikhala ndi Alevi, polandira Alevi limodzilimodzi la magawo khumi; ndi Alevi azikwera nalo limodzi la magawo khumi mwa limodzilimodzi la magawo khumi kunyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda, kunyumba ya chuma.
39 Pakuti ana a Israele ndi ana a Levi, azibwera nayo nsembe yokweza yatirigu, ndi yavinyo ndi yamafuta, kuzipinda kuli zipangizo za malo opatulika, ndi ansembe akutumikira, ndi odikira, ndi oimbira; kuti tisasiye nyumba ya Mulungu wathu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NEH/10-e2907d3749ba6ac9a9dd19e9230ebcd2.mp3?version_id=1068—