Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 8

Nzeru ipambana m’kuchita kwake

1 Kodi nzeru siitana,

luntha ndi kukweza mau ake?

2 Iima pamwamba pa mtunda,

pa mphambano za makwalala;

3 pambali pa chipata polowera m’mudzi,

polowa anthu pa makomo ifuula:

4 Ndinu ndikuitanani, amuna,

mau anga ndilankhula kwa ana a anthu.

5 Achibwana inu, chenjerani,

opusa inu, khalani ndi mtima wozindikira;

6 imvani, pakuti ndikanena zoposa,

ndi zolungama potsegula pakamwa panga.

7 Pakuti m’kamwa mwanga mudzalankhula ntheradi,

zoipa zinyansa milomo yanga.

8 Mau onse a m’kamwa mwanga alungama;

mwa iwo mulibe zokhota ndi zopotoka.

9 Onsewo amveka ndi iye amene azindikira;

alungama kwa akupeza nzeru.

10 Landirani mwambo wanga, sisilivaai;

ndi nzeru kopambana ndi golide wosankhika.

11 Pakuti nzeru iposa ngale,

ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo.

12 Ine Nzeru ndikhala m’kuchenjera, ngati m’nyumba yanga;

ndimapeza kudziwa ndi zolingalira.

13 Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa;

kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa,

ndi m’kamwa mokhota, ndizida.

14 Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa;

ndine luntha; ndili ndi mphamvu.

15 Mwa ine mafumu alamulira;

akazembe naweruza molungama.

16 Mwa ine akalonga ayang’anira,

ndi akulu, ngakhale oweruza onse a m’dziko.

17 Akundikonda ndiwakonda;

akundifunafuna adzandipeza.

18 Katundu ndi ulemu zili ndi ine,

chuma chosatha ndi chilungamo.

19 Chipatso changa chiposa golide, ngakhale golide woyengeka;

phindu langa liposa siliva wosankhika.

20 Ndimayenda m’njira ya chilungamo,

pakati pa mayendedwe a chiweruzo,

21 kuti ndionetse chuma akundikonda, chikhale cholowa chao,

ndi kudzaza mosungira mwao.

Nzeru ndiyo ya nthawi yosayamba

22 Yehova anali nane poyamba njira yake,

asanalenge zake zakale.

23 Anandiimika chikhalire chiyambire,

dziko lisanalengedwe.

24 Pamene panalibe zozama ndinabadwa ine,

pamene panalibe akasupe odzala madzi.

25 Mapiri asanakhazikike,

zitunda zisanapangidwe, ndinabadwa.

26 Asanalenge dziko, ndi thengo,

ngakhale chiyambi cha fumbi la dziko.

27 Pamene anakhazika mlengalenga ndinali pompo;

pamene analemba pazozama kwetekwete;

28 polimbitsa Iye thambo la kumwamba,

pokula akasupe a zozama.

29 Poikira nyanja malire ake,

kuti madzi asapitirire pa lamulo lake;

polemba maziko a dziko.

30 Ndinali pa mbali pake ngati mmisiri;

ndinamsekeretsa tsiku ndi tsiku,

ndi kukondwera pamaso pake nthawi zonse;

31 ndi kukondwera ndi dziko lake lokhalamo anthu,

ndi kusekerera ndi ana a anthu.

32 Ndipo tsopano, ananga, mundimvere ine,

ngodala akusunga njira zanga.

33 Imvani mwambo, mukhale anzeru osaukana.

34 Ngwodala amene andimvera,

nadikira pa zitseko zanga tsiku ndi tsiku,

ndi kulinda pa mphuthu za makoma anga;

35 pakuti wondipeza ine apeza moyo;

Yehova adzamkomera mtima.

36 Koma wondichimwira apweteka moyo wake;

onse akundida ine akonda imfa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/8-65b70aedaa5e09db561e00a6b605e874.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *