Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 3

Malangizo a kuopa, kukhulupirira, ndi kumvera Yehova

1 Mwananga, usaiwale malamulo anga,

mtima wako usunge malangizo anga;

2 pakuti adzakuonjezera masiku ambiri,

ndi zaka za moyo ndi mtendere.

3 Chifundo ndi choonadi zisakusiye;

uzimange pakhosi pako;

uzilembe pamtima pako;

4 motero udzapeza chisomo ndi nzeru yabwino,

pamaso pa Mulungu ndi anthu.

5 Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse,

osachirikizika pa luntha lako;

6 umlemekeze m’njira zako zonse,

ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

7 Usadziyese wekha wanzeru;

opa Yehova, nupatuke pazoipa;

8 mitsempha yako idzalandirapo moyo,

ndi mafupa ako uwisi.

9 Lemekeza Yehova ndi chuma chako,

ndi zinthu zako zonse zoyambirira kucha;

10 motero nkhokwe zako zidzangoti thee,

mbiya zako zidzasefuka vinyo.

11 Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,

ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwake;

12 pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;

monga atate mwana amene akondwera naye.

Phindu la Nzeru

13 Wodala ndi wopeza nzeru,

ndi woona luntha;

14 pakuti malonda a nzeru aposa malonda asiliva,

phindu lake liposa golide woyengeka.

15 Mtengo wake uposa ngale;

ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.

16 Masiku ambiri ali m’dzanja lamanja lake;

chuma ndi ulemu m’dzanja lake lamanzere.

17 Njira zake zili zokondweretsa,

mayendedwe ake onse ndiwo mtendere.

18 Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira;

wakuiumirira ngwodala.

19 Yehova anakhazika dziko ndi nzeru;

naika zamwamba ndi luntha.

20 Zakuya zinang’ambika ndi kudziwa kwake;

thambo ligwetsa mame.

21 Mwananga, zisachokere kumaso ako;

sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;

22 ndipo mtima wako udzatengapo moyo,

ndi khosi lako chisomo.

23 Pompo udzayenda m’njira yako osaopa,

osaphunthwa phazi lako.

24 Ukagona, sudzachita mantha;

udzagona tulo tokondweretsa.

25 Usaope zoopsa zodzidzimutsa,

ngakhale zikadza zopasula oipa;

26 pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako,

nadzasunga phazi lako lingakodwe.

Malangizo ena osiyana

27 Oyenera kulandira zabwino usawamane;

pokhoza dzanja lako kuwachitira zabwino.

28 Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso,

ndipo mawa ndidzakupatsa;

pokhala uli nako kanthu.

29 Usapangire mnzako chiwembu;

popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.

30 Usakangane ndi munthu chabe,

ngati sanakuchitire choipa.

31 Usachitire nsanje munthu wachiwawa;

usasankhe njira yake iliyonse.

32 Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova;

koma chinsinsi chake chili ndi oongoka.

33 Yehova atemberera za m’nyumba ya woipa;

koma adalitsa mokhalamo olungama.

34 Anyozadi akunyoza,

koma apatsa akufatsa chisomo.

35 Anzeru adzalandira ulemu cholowa chao;

koma opusa adzakweza manyazi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/3-e517f48ff8327cd8228c94a3e6c5b797.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *