Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 2

Ukoma ndi phindu lake la Nzeru

1 Mwananga, ukalandira mau anga,

ndi kusunga malamulo anga;

2 kutcherera makutu ako kunzeru,

kulozetsa mtima wako kukuzindikira;

3 ukaitananso luntha,

ndi kufuulira kuti ukazindikire;

4 ukaifunafuna ngatisiliva,

ndi kuipwaira ngati chuma chobisika;

5 pompo udzazindikira kuopa Yehova

ndi kumdziwadi Mulungu.

6 Pakuti Yehova apatsa nzeru;

kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m’kamwa mwake.

7 Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni;

ndiye chikopa cha oyenda molunjika;

8 kuti atchinjirize njira za chiweruzo,

nadikire khwalala la opatulidwa ake.

9 Pamenepo udzazindikira chilungamo ndi chiweruzo,

zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.

10 Pakuti nzeru idzalowa m’mtima mwako,

moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

11 kulingalira kudzakudikira,

kuzindikira kudzakutchinjiriza;

12 kukupulumutsa kunjira yoipa,

kwa anthu onena zokhota;

13 akusiya mayendedwe olungama,

akayende m’njira za mdima;

14 omwe asangalala pochita zoipa,

nakondwera ndi zokhota zoipa;

15 amene apotoza njira zao,

nakhotetsa mayendedwe ao.

16 Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi wachiwerewere,

kwa mkazi wachilendo wosyasyalika ndi mau ake;

17 wosiya bwenzi la ubwana wake,

naiwalachipanganocha Mulungu wake.

18 Nyumba yake itsikira kuimfa,

ndi mayendedwe ake kwa akufa;

19 onse akunka kwa iye sabweranso,

safika kunjira za moyo;

20 nzeru idzakuyendetsa m’njira ya anthu abwino,

kuti usunge mayendedwe a olungama.

21 Pakuti oongoka mtima adzakhala m’dziko,

angwiro nadzatsalamo.

22 Koma oipa adzalikhidwa m’dziko,

achiwembu adzazulidwamo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/2-cf23f208ad1a7192340fc8e2c2fe8d53.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *