Ukoma ndi phindu lake la Nzeru
1 Mwananga, ukalandira mau anga,
ndi kusunga malamulo anga;
2 kutcherera makutu ako kunzeru,
kulozetsa mtima wako kukuzindikira;
3 ukaitananso luntha,
ndi kufuulira kuti ukazindikire;
4 ukaifunafuna ngatisiliva,
ndi kuipwaira ngati chuma chobisika;
5 pompo udzazindikira kuopa Yehova
ndi kumdziwadi Mulungu.
6 Pakuti Yehova apatsa nzeru;
kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m’kamwa mwake.
7 Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni;
ndiye chikopa cha oyenda molunjika;
8 kuti atchinjirize njira za chiweruzo,
nadikire khwalala la opatulidwa ake.
9 Pamenepo udzazindikira chilungamo ndi chiweruzo,
zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.
10 Pakuti nzeru idzalowa m’mtima mwako,
moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,
11 kulingalira kudzakudikira,
kuzindikira kudzakutchinjiriza;
12 kukupulumutsa kunjira yoipa,
kwa anthu onena zokhota;
13 akusiya mayendedwe olungama,
akayende m’njira za mdima;
14 omwe asangalala pochita zoipa,
nakondwera ndi zokhota zoipa;
15 amene apotoza njira zao,
nakhotetsa mayendedwe ao.
16 Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi wachiwerewere,
kwa mkazi wachilendo wosyasyalika ndi mau ake;
17 wosiya bwenzi la ubwana wake,
naiwalachipanganocha Mulungu wake.
18 Nyumba yake itsikira kuimfa,
ndi mayendedwe ake kwa akufa;
19 onse akunka kwa iye sabweranso,
safika kunjira za moyo;
20 nzeru idzakuyendetsa m’njira ya anthu abwino,
kuti usunge mayendedwe a olungama.
21 Pakuti oongoka mtima adzakhala m’dziko,
angwiro nadzatsalamo.
22 Koma oipa adzalikhidwa m’dziko,
achiwembu adzazulidwamo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/2-cf23f208ad1a7192340fc8e2c2fe8d53.mp3?version_id=1068—