Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 12

1 Wokonda mwambo akonda kudziwa;

koma wakuda chidzudzulo apulukira.

2 Yehova akomera mtima munthu wabwino;

koma munthu wa ziwembu amtsutsa.

3 Munthu sadzakhazikika ndi udyo,

muzu wa olungama sudzasunthidwa.

4 Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wake;

koma wochititsa manyazi akunga chovunditsa mafupa a mwamunayo.

5 Maganizo a olungama ndi chiweruzo;

koma uphungu wa oipa unyenga.

6 Mau a oipa abisalira mwazi;

koma m’kamwa mwa olungama muwalanditsa.

7 Oipa amagwa kuli zii;

koma banja la olungama limaimabe.

8 Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yake;

koma wokhota mtima adzanyozedwa.

9 Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,

aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.

10 Wolungama asamalira moyo wa choweta chake;

koma chifundo cha oipa ndi nkhanza.

11 Zakudya zikwanira wolima minda yake;

koma wotsata anthu opanda pake asowa nzeru.

12 Woipa akhumba chokodwa ndi amphulupulu;

koma muzu wa olungama umabala zipatso.

13 M’kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;

koma wolungama amatuluka m’mavuto.

14 Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m’kamwa mwake;

zochita za manja ake zidzabwezedwa kwa iye.

15 Njira ya chitsiru njolungama pamaso pakepake;

koma wanzeru amamvera uphungu.

16 Mkwiyo wa chitsiru udziwika posachedwa;

koma wanzeru amabisa manyazi.

17 Wolankhula ntheradi aonetsa chilungamo;

koma mboni yonama imanyenga.

18 Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;

koma lilime la anzeru lilamitsa.

19 Mlomo wa ntheradi ukhazikika nthawi zonse;

koma lilime lonama likhala kamphindi.

20 Chinyengo chili m’mitima ya oganizira zoipa;

koma aphungu a mtendere amakondwa.

21 Palibe vuto lidzagwera wolungama;

koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa.

22 Milomo yonama inyansa Yehova;

koma ochita ntheradi amsekeretsa.

23 Munthu wanzeru abisa zomwe adziwa;

koma mtima wa opusa ulalikira utsiru.

24 Dzanja la akhama lidzalamulira;

koma waulesi adzakhala ngati kapolo.

25 Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu;

koma mau abwino aukondweretsa.

26 Wolungama atsogolera mnzake;

koma njira ya oipa iwasokeretsa.

27 Waulesi samaotcha nyama yake anaigwira;

koma wolungama amalandira chuma chopambana cha anthu.

28 M’khwalala la chilungamo muli moyo;

m’njira ya mayendedwe ake mulibe imfa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/12-a208f60d659d30d94ba0fd02c30d5dc5.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *