Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 11

1 Muyeso wonyenga unyansa Yehova;

koma mulingo wamphumphu umsekeretsa.

2 Pakudza kudzikuza padzanso manyazi;

koma nzeru ili ndi odzichepetsa.

3 Kuongoka mtima kwa olungama kuwatsogolera;

koma kukhota kwa achiwembu kudzawaononga.

4 Chuma sichithandiza tsiku la mkwiyo;

koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.

5 Chilungamo cha wangwiro chimaongola njira yake;

koma woipa adzagwa ndi zoipa zake.

6 Chilungamo cha oongoka mtima chidzawapulumutsa;

koma achiwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.

7 Pomwalira woipa chidikiro chake chionongeka;

chiyembekezo cha uchimo chionongeka.

8 Wolungama apulumuka kuvuto;

woipa nalowa m’malo mwake.

9 Wonyoza Mulungu aononga mnzake ndi m’kamwa mwake;

koma olungama adzapulumuka pakudziwa.

10 Olungama akapeza bwino, mzinda usekera;

nufuula pakuonongeka oipa.

11 Madalitso a olungama akuza mzinda;

koma m’kamwa mwa oipa muupasula.

12 Wopeputsa mnzake asowa nzeru;

koma wozindikira amatonthola.

13 Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi;

koma wokhulupirika mtima abisa mau.

14 Popanda upo wanzeru anthu amagwa;

koma pochuluka aphungu pali chipulumutso.

15 Woperekera mlendo chikole adzaphwetekwapo;

koma wakuda chikole akhala ndi mtendere.

16 Mkazi wodekha agwiritsa ulemu;

aukali nagwiritsa chuma.

17 Wachifundo achitira moyo wake zokoma;

koma wankhanza avuta nyama yake.

18 Woipa alandira malipiro onyenga;

koma wofesa chilungamo aonadi mphotho.

19 Wolimbikira chilungamo alandira moyo;

koma wolondola zoipa adzipha yekha.

20 Okhota mtima anyansa Yehova;

koma angwiro m’njira zao amsekeretsa.

21 Zoonadi, wochimwa sadzapulumuka chilango;

koma mbeu ya olungama idzalanditsidwa.

22 Monga chipini chagolide m’mphuno ya nkhumba,

momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.

23 Chifuniro cha olungama chifikitsa zabwino zokha;

koma chiyembekezo cha oipa mkwiyo.

24 Alipo wogawira, nangolemerabe;

aliponso womana chomwe ayenera kupatsa nangosauka.

25 Mtima wa mataya udzalemera;

wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

26 Womana tirigu anthu amtemberera;

koma madalitso adzakhala pamutu pa wogulitsa.

27 Wopwaira ubwino afunitsa chikondwerero;

koma zoipa zidzamfikira wozilondola.

28 Wokhulupirira chuma chake adzagwa;

koma olungama adzaphuka ngati tsamba.

29 Wovuta banja lake adzalowa m’zomsautsa;

wopusa adzatumikira wanzeru.

30 Chipatso cha wolungama ndi mtengo wa moyo;

ndipo wokola mtima ali wanzeru.

31 Taonani, wolungama adzalandira mphotho kunja kuno;

koposa kotani woipa ndi wochimwa?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/11-3a2dfc12137683cdafeb18a644d55365.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *