Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 10

Miyambo yosiyanasiyana

Miyambo ya Solomoni:

1 Mwana wanzeru akondweretsa atate;

koma mwana wopusa amvetsa amake chisoni.

2 Chuma cha uchimo sichithangata;

koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.

3 Yehova samvetsa njala moyo wa wolungama;

koma amainga chifuniro cha wochimwa.

4 Wochita ndi dzanja laulesi amasauka;

koma dzanja la akhama lilemeretsa.

5 Wokolola m’malimwe ndi mwana wanzeru;

koma wogona pakututa ndi mwana wochititsa manyazi.

6 Madalitso ali pamutu pa wolungama;

koma m’kamwa mwa oipa mubisa chiwawa.

7 Amayesa wolungama wodala pomkumbukira;

koma dzina la oipa lidzavunda.

8 Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;

koma chitsiru cholongolola chidzagwa.

9 Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;

koma wokhotetsa njira zake adzadziwika.

10 Wotsinzinira achititsa chisoni;

koma wodzudzula momveka achita mtendere.

11 M’kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;

koma m’kamwa mwa oipa mubisa chiwawa.

12 Udani upikisanitsa;

koma chikondi chikwirira zolakwa zonse.

13 Nzeru ipezedwa m’milomo ya wozindikira;

koma wopusa pamsana pake nthyole.

14 Anzeru akundika zomwe adziwa;

koma m’kamwa mwa chitsiru muononga tsopano lino.

15 Chuma cha wolemera ndi mzinda wake wolimba;

koma umphawi wao uononga osauka.

16 Ntchito za wolungama zipatsa moyo;

koma phindu la oipa lichimwitsa.

17 Wosunga mwambo ali m’njira ya moyo;

koma wosiya chidzudzulo asochera.

18 Wobisa udani ali ndi milomo yonama;

wonena ugogodi ndiye chitsiru.

19 Pochuluka mau zolakwa sizisoweka;

koma wokhala chete achita mwanzeru.

20 Lilime la wolungama likungasilivawosankhika;

koma mtima wa oipa uli wachabe.

21 Milomo ya wolungama imadyetsa ambiri;

koma zitsiru zimafa posowa nzeru.

22 Madalitso a Yehova alemeretsa,

saonjezerapo chisoni.

23 Masewero a chitsiru ndiwo kuchita zoipa;

koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.

24 Chomwe woipa achiopa chidzamfikira;

koma chomwe olungama achifuna chidzapatsidwa.

25 Monga kavumvulu angopita, momwemo woipa kuli zii;

koma olungama ndiwo maziko osatha.

26 Ngati vinyo wowawa m’mano, ndi utsi m’maso,

momwemo waulesi kwa iwo amene amtuma.

27 Kuopa Yehova kutanimphitsa masiku;

koma zaka za oipa zidzafinimpha.

28 Chiyembekezo cha olungama ndicho chimwemwe;

koma chidikiro cha oipa chidzaonongeka.

29 Njira ya Yehova ndi linga kwa woongoka mtima;

koma akuchita zoipa adzaonongeka.

30 Wolungama sadzachotsedwa konse;

koma oipa sadzakhalabe m’dziko.

31 M’kamwa mwa wolungama mulankhula nzeru;

koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32 Milomo ya wolungama idziwa zokondweretsa;

koma m’kamwa mwa oipa munena zokhota.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/10-6640647a67135114988aab0e34b398f7.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *