Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 1

Zochitira miyambo

1 Miyambo ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israele.

2 Kudziwa nzeru ndi mwambo;

kuzindikira mau ozindikiritsa;

3 kulandira mwambo wakusamalira machitidwe,

chilungamo, chiweruzo ndi zolunjika;

4 kuchenjeza achibwana,

kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;

5 kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira;

ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;

6 kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lake,

mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.

Munthu asalole oipa amchete

7 Kuopa Yehova ndiko chiyambi cha kudziwa;

opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

8 Mwananga, tamva mwambo wa atate wako,

ndi kusasiya chilangizo cha amai ako;

9 pakuti izi ndi korona wa chisomo pamutu pako,

ndi mkanda pakhosi pako.

10 Mwananga, akakukopa ochimwa usalole.

11 Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi,

tilalire osachimwa opanda chifukwa;

12 tiwameze ali ndi moyo ngati manda,

ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;

13 tidzapeza chuma chonse cha mtengo wake,

tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;

14 udzachita nafe maere,

tonse tidzakhala ndi chotengeramo chimodzi.

15 Mwananga, usayende nao m’njira;

letsa phazi lako ku mayendedwe ao;

16 pakuti mapazi ao athamangira zoipa,

afulumira kukhetsa mwazi.

17 Pakuti kutchera msampha pamaso pa mbalame ndi chabe;

18 ndipo awa abisalira mwazi waowao, alalira miyoyo yaoyao.

19 Mayendedwe a yense wopindula chuma monyenga ngotere;

chilanda moyo wa eni ake.

Chenjezo la Nzeru

20 Nzeru ifuula panja;

imveketsa mau ake pabwalo;

21 iitana posonkhana anthu polowera pachipata;

m’mzinda inena mau ake,

22 Kodi mudzakonda zazibwana kufikira liti, achibwana inu?

Onyoza ndi kukonda kunyoza,

opusa ndi kuda nzeru?

23 Tembenukani pamene ndikudzudzulani;

taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga,

ndikudziwitsani mau anga.

24 Chifukwa ndaitana, ndipo munakana;

ndatambasula dzanja langa,

ndipo panalibe analabadira;

25 koma munapeputsa uphungu wanga wonse,

ndi kukana kudzudzula kwanga.

26 Inetu ndidzachitira chiphwete tsoka lanu,

ndidzatonyola pakudza mantha anu;

27 pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula,

ndi pofika tsoka lanu ngati kamvulumvulu;

pakudza kwa inu vuto ndi nsautso.

28 Pamenepo adzandiitana,

koma sindidzavomera;

adzandifunatu, osandipeza ai;

29 chifukwa anada nzeru,

sanafune kuopa Yehova;

30 anakana uphungu wanga,

nanyoza kudzudzula kwanga konse;

31 momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao,

nadzakhuta zolingalira zao.

32 Pakuti kubwerera m’mbuyo kwa achibwana kudzawapha;

ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.

33 Koma wondimvera ine adzakhala osatekeseka,

nadzakhala phee osaopa zoipa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/1-32cef618ad9ecae5edf89bcb3338ccd7.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *