Categories
MIKA

MIKA 1

Mau akuchenjeza Israele ndi Yuda chifukwa cha machimo ao

1 Mau a Yehova amene anadza kwa Mika wa ku Moreseti masiku a Yotamu, Ahazi, ndi Hezekiya, mafumu a Yuda, amene adaona za Samariya ndiYerusalemu.

2 Imvani, mitundu ya anthu, inu nonse; tamvera, dziko lapansi, ndi zonse zili m’mwemo; ndipo Ambuye Yehova akhale mboni yakutsutsa inu, Ambuye mu Kachisi wake wopatulika.

3 Pakuti, taonani, Yehova alikutuluka m’malo mwake, nadzatsika, nadzaponda pa misanje ya dziko lapansi.

4 Ndi mapiri adzasungunuka pansi pa Iye, ndi zigwa zidzang’ambika, ngati sera pamoto, ngati madzi otsanulidwa potsetsereka.

5 Chichitika ichi chonse chifukwa cha kulakwa kwa Yakobo, ndi machimo a nyumba ya Israele. Kulakwa kwa Yakobo nkotani? Si ndiko Samariya? Ndi misanje ya Yuda ndi iti? Si ndiyo Yerusalemu?

6 Chifukwa chake ndidzaika Samariya ngati mulu wa miyala ya m’munda, ngati zooka m’munda wampesa; ndipo ndidzataya miyala yake m’chigwa, ndi kufukula maziko ake.

7 Ndi mafano ake osema onse adzaphwanyika, ndi mphotho zake zonse zidzatenthedwa ndi moto, ndi mafano ake onse ndidzawapasula; pakuti anazisonkhanitsa pa mphotho ya mkazi wachiwerewere, ndipo zidzabwerera kumphotho ya mkazi wachiwerewere.

8 Chifukwa cha ichi ndidzachita maliro, ndi kuchema, ndidzayenda wolandidwa ndi wamaliseche; ndidzalira ngati nkhandwe, ndi kubuma ngati nthiwatiwa.

9 Pakuti mabala ake ndi osapola; pakuti afikira ku Yuda; afikira ku chipata cha anthu anga, ku Yerusalemu.

10 Musachifotokoza mu Gati, musalira misozi konse; m’nyumba ya Afira ndinagubuduka m’fumbi.

11 Pitiratu, wokhala mu Safiri iwe, wamaliseche ndi wamanyazi; wokhala mu Zanani sanatuluke; maliro a Betezele adzakulandani pokhala pake.

12 Pakuti wokhala mu Maroti alindira chokoma, popeza choipa chatsika kwa Yehova kunka kuchipata cha Yerusalemu.

13 Manga galeta kukavalo waliwiro, wokhala mu Lakisi iwe, woyamba kuchimwitsa mwana wamkazi waZiyonindi iye; pakuti zolakwa za Israele zinapezedwa mwa iwe.

14 Chifukwa chake pereka mphatso zolawirana kwa Moreseti-Gati; nyumba za Akizibu zidzakhala chinthu chabodza kwa mafumu a Israele.

15 Ndidzakutengeranso wokhala mu Maresa iwe, iye amene adzakulandira ukhale cholowa chake; ulemerero wa Israele udzafikira ku Adulamu.

16 Udziyeseze wadazi, udzimete wekha chifukwa cha ana ako okondwera nao; kuza dazi lako ngati la muimba; pakuti anakuchokera, nalowa ndende.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MIC/1-dd0804d9b0b670726b7ec842db775a3e.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *