Yudasi adzipachika yekha
1 Ndipo pakudza mamawa, ansembe aakulu ndi akulu a anthu onse anakhala upo wakumchitira Yesu, kuti amuphe;
2 ndipo anammanga Iye, namuka naye, nampereka Iye kwa Pilato kazembeyo.
3 Pamenepo Yudasi yemwe anampereka Iye, poona kuti Iye anatsutsidwa kuti afe, analapa, nabweza ndalama zija zasilivamakumi atatu kwa ansembe aakulu ndi akulu,
4 nanena, Ndinachita koipa ine, pakupereka mwazi wosalakwa. Koma iwo anati, Tili nacho chiyani ife? Udzionere wekha.
5 Ndipo iye anataya pansi ndalamazo pa Kachisi, nachokapo, nadzipachika yekha pakhosi.
6 Ndipo ansembe aakulu anatenga ndalamazo, nati, Sikuloledwa kuziika m’chosonkhera ndalama za Mulungu, chifukwa ndizo mtengo wa mwazi.
7 Koma anapangana, nazigula munda wa woumba mbiya, ukhale manda a alendo.
8 Chifukwa chake munda umenewu anautcha, Munda-wa-mwazi, kufikira lero lino.
9 Pamenepo chinakwaniridwa chonenedwa ndi Yeremiyamneneri, ndi kuti,
Ndipo iwo anatenga ndalamazo zasiliva makumi atatu,
mtengo wa uja wowerengedwa mtengo wake,
amene iwo a ana a Israele anawerenga mtengo wake;
10 ndipo anazipereka kugula munda wa woumba mbiya,
monga anandilamulira ine Ambuye.
Yesu kwa Pilato
11 Ndipo Yesu anaimirira pamaso pa kazembe, ndipo kazembeyo anamfunsa Iye kuti, Kodi Iwe ndiwe mfumu ya Ayuda? Ndipo Yesu anati kwa iye, Mwatero.
12 Ndipo pakumnenera Iye ansembe aakulu ndi akulu, Iye sanayankhe kanthu.
13 Pomwepo Pilato ananena kwa Iye, Sukumva kodi zinthu zambiri zotere akunenera Iwe?
14 Ndipo sanayankhe Iye, ngakhale mau amodzi, kotero kuti kazembe anazizwa ndithu.
15 Ndipo pa chikondwerero kazembe adazolowera kumasulira anthu mmodzi wandende, amene iwo anafuna.
16 Ndipo pa nthawi yomweyo anali ndi wandende wodziwika, dzina lake Barabasi.
17 Chifukwa chake pamene anasonkhana, Pilato ananena kwa iwo, Mufuna kuti ndikumasulireni yani? Barabasi kodi, kapena Yesu, wotchedwaKhristu?
18 Pakuti anadziwa kuti anampereka Iye mwanjiru.
19 Ndipo pamene Pilato analikukhala pa mpando wakuweruza, mkazi wake anatumiza mau kwa iye, kunena, Musachite kanthu ndi munthu wolungamayo; pakuti lero m’kulota ine ndasauka kwambiri chifukwa cha Iye.
20 Koma ansembe aakulu ndi akulu anapangira anthu kuti apemphe Barabasi, koma kuti aononge Yesu.
21 Koma kazembe anati kwa iwo, Mufuna kuti ndikumasulireni uti wa awa awiri? Ndipo iwo anati, Barabasi.
22 Pilato ananena kwa iwo, Nanga ndidzachita chiyani ndi Yesu, wotchedwa Khristu? Onse anati, Apachikidwe pamtanda.
23 Ndipo iye anati, Chifukwa ninji? Anachita choipa chotani? Koma iwo anafuulitsa kopambana, Apachikidwe pamtanda.
24 Koma Pilato poona kuti sanafitse, koma kuti linapambana phokoso, anatenga madzi, nasamba manja pamaso pa khamulo, nati, Ine ndilibe kuchimwira mwazi wa munthu uyu wolungama, mudzionere nokha.
25 Ndipo anthu onse anavomereza, ndi kuti, Mwazi wake uli pa ife ndi pa ana athu.
26 Pomwepo iye anamasulira iwo Barabasi, koma anakwapula Yesu, nampereka Iye kuti akampachike pamtanda.
27 Pomwepo asilikali a kazembe anamuka naye Yesu kubwalo la milandu, nasonkhanitsa kwa Iye khamu lao lonse.
28 Ndipo anavula malaya ake, namveka malaya ofiira achifumu.
29 Ndipo analuka korona waminga, namveka pamutu pake, namgwiritsa bango m’dzanja lamanja lake; ndipo anagwada pansi pamaso pake, namchitira chipongwe, nati, Tikuoneni, mfumu ya Ayuda!
30 Namthira malovu, natenga bango, nampanda Iye pamutu.
31 Ndipo pamene anatha kumchitira Iye chipongwe, anavula malaya aja, namveka Iye malaya ake, natsogoza Iye kukampachika pamtanda.
Ampachika Yesu
32 Ndipo pakutuluka pao anapeza munthu wa ku Kirene, dzina lake Simoni, namkakamiza iye kuti anyamule mtanda wake.
33 Ndipo pamene anadza kumalo dzina lake Gologota, ndiko kunena kuti, Malo a Bade,
34 anamwetsa Iye vinyo wosakaniza ndi ndulu; ndipo Iye, m’mene analawa, sanafune kumwa.
35 Ndipo pamene anampachika Iye, anagawana zovala zake ndi kulota maere:
36 nakhala iwo pansi, namdikira kumeneko.
37 Ndipo anaika pamwamba pamutu pake mlandu wake wolembedwa: UYU NDI YESU MFUMU YA AYUDA.
38 Pamenepo anapachika pamodzi ndi Iye achifwamba awiri, mmodzi kudzanja lamanja, ndi wina kulamanzere.
39 Ndipo anthu akupitirirapo anamchitira mwano Iye ndi kupukusa mitu yao,
40 nati, Nanga Iwe, wopasula Kachisi, ndi kummanganso masiku atatu, tadzipulumutsa wekha; ngati uli Mwana wa Mulungu, tatsika pamtandapo.
41 Chomwechonso ansembe aakulu, pamodzi ndi alembi ndi akulu anamchitira chipongwe, nati,
42 Anapulumutsa ena, sangathe kudzipulumutsa yekha. Ndiye mfumu ya Aisraele; atsike tsopano pamtandapo, ndipo tidzamkhulupirira Iye.
43 Amakhulupirira Mulungu; Iye ampulumutse tsopano, ngati amfuna; pakuti anati, Ine ndine Mwana wa Mulungu.
44 Ndiponso achifwambawo opachikidwa pamodzi ndi Iye, anamlalatira Iye mau amodzimodzi.
45 Ndipo ora lachisanu ndi chimodzi panali mdima padziko lonse, kufikira ora lachisanu ndi chinai.
46 Ndipo poyandikira ora lachisanu ndi chinai, Yesu anafuula ndi mau aakulu, kunena,Eli, Eli, lama sabakitani?ndiko kunena kuti, Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji Ine?
47 Ndipo ena a iwo akuimirira komweko, pamene anamva, ananena, Uyo aitana Eliya.
48 Ndipo pomwepa mmodzi wa iwo anathamanga, natenga chinkhupule, nachidzaza ndi vinyo wosasa, nachiika pabango, namwetsa Iye.
49 Koma ena anati, Taleka, tione ngati Eliya adzafika kudzampulumutsa.
50 Ndipo Yesu, pamene anafuula ndi mau aakulu, anapereka mzimu wake.
51 Ndipo onani, chinsalu chotchinga cha mu Kachisi chinang’ambika pakati, kuchokera kumwamba kufikira pansi; ndipo dziko linagwedezeka, ndi miyala inang’ambika;
52 ndi manda anatseguka, ndi mitembo yambiri ya anthu oyera mtima, akugona kale, inauka;
53 ndipo anatuluka m’manda mwao pambuyo pa kuuka kwake, nalowa m’mzinda woyera, naonekera kwa anthu ambiri.
54 Ndipo anali naye akudikira Yesu, anaona chivomezi, ndi zinthu zimene zinachitidwa, anaopa kwambiri, nanena, Indedi Uyu ndiye Mwana wa Mulungu.
55 Ndipo anali pomwepo akazi ambiri, akuyang’anira patali, omwe anatsata Yesu kuchokera ku Galileya, namatumikira Iye;
56 mwa iwo amene munali Maria wa Magadala, ndi Maria amake wa Yakobo, ndi wa Yosefe, ndi amake wa ana a Zebedeo.
Amuika Yesu kumanda
57 Ndipo pamene panali madzulo, anadza munthu wachuma wa ku Arimatea, dzina lake Yosefe, amene analinso wophunzirawa Yesu;
58 yemweyo anapita kwa Pilato, napempha mtembo wa Yesu. Pomwepo Pilato analamula kuti uperekedwe.
59 Ndipo Yosefe anatenga mtembo, naukulunga m’nsalu yabafuta yoyeretsa,
60 nauika m’manda ake atsopano, osemedwa m’mwala, nakunkhunizira mwala waukulu pakhomo pa manda, nachokapo.
61 Ndipo Maria wa Magadala anali pamenepo, ndi Maria winayo, anakhala pansi popenyana ndi mandawo.
62 Ndipo m’mawa mwake, ndilo tsiku lotsatana ndi tsiku lokonzera, ansembe aakulu ndiAfarisianasonkhana kwa Pilato,
63 nanena, Mfumu, takumbukira ife kuti wonyenga uja anati, pamene anali ndi moyo, Ndidzauka pofika masiku atatu.
64 Chifukwa chake mulamule kuti asindikize pamandapo, kufikira tsiku lachitatulo, kuti kapenaophunziraake angadze, nadzamuba Iye, nadzanena kwa anthu, kuti Iye anauka kwa akufa: ndipo chinyengo chomaliza chidzaposa choyambacho.
65 Pilato anati kwa iwo, Tengani alonda; mukani, kasungeni monga mudziwa.
66 Ndipo iwo anamuka, nasunga manda, nasindikizapo chizindikiro pamwalapo, iwo pamodzi ndi alondawo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAT/27-22074afdf55f92e99978acaeae04aa61.mp3?version_id=1068—