Categories
MATEYU

MATEYU 23

Yesu adzudzula Alembi ndi Afarisi

1 Pomwepo Yesu analankhula ndi makamu a anthu ndiophunziraake,

2 nanena, Alembi ndiAfarisiakhala pa mpando wa Mose;

3 chifukwa chake zinthu zilizonse zimene iwo akauza inu, chitani nimusunge; koma musatsanza ntchito zao; pakuti iwo amalankhula, koma samachita.

4 Inde, amanga akatundu olemera ndi osautsa ponyamula, nawasenza pa mapewa a anthu; koma iwo eni okha safuna kuwasuntha amenewo ndi chala chao.

5 Koma amachita ntchito zao zonse kuti aonekere kwa anthu; pakuti akulitsa chitando chake cha njirisi zao, nakulitsa mphonje,

6 nakonda malo a ulemu pamaphwando, ndi mipando ya ulemu m’masunagoge,

7 ndi kulonjeredwa m’misika, ndi kutchedwa ndi anthu,Rabi.

8 Koma inu musatchedwa Rabi; pakuti Mphunzitsi wanu ali mmodzi, ndipo inu nonse muli abale.

9 Ndipo inu musatchule wina atate wanu pansi pano, pakuti alipo mmodzi ndiye Atate wanu wa Kumwamba.

10 Ndipo musatchedwa atsogoleri, pakuti alipo mmodzi Mtsogoleri wanu, ndiye Khristu.

11 Koma wamkulu wopambana wa inu adzakhala mtumiki wanu.

12 Ndipo aliyense amene akadzikuza yekha adzachepetsedwa; koma amene adzichepetsa mwini yekha adzakulitsidwa.

13 Koma tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! Chifukwa mutsekera anthu Ufumu wa Kumwamba pamaso pao; pakuti inu nokha simulowamo, ndipo muwaletsa amene alikulowa, kuti asalowemo.

15 Tsoka inu alembi ndi Afarisi, onyenga! Chifukwa mupitapita kunyanja ndi kumtunda kuyesa munthu mmodzi mtembenuki; ndipo m’mene akhala wotere, mumsandutsa mwana waGehenawoposa inu kawiri.

16 Tsoka inu, atsogoleri akhungu, amene munena, Amene aliyense akalumbira kutchula Kachisi, palibe kanthu; koma amene akalumbira kutchula golide wa Kachisi, wadzimangirira.

17 Inu opusa, ndi akhungu: pakuti choposa nchiti, golide kodi, kapena Kachisi amene ayeretsa golideyo?

18 Ndiponso, Amene aliyense akalumbira kutchula guwa la nsembe, palibe kanthu; koma amene akalumbira kutchula mtulo wa pamwamba pake wadzimangirira.

19 Inu akhungu, pakuti choposa nchiti, mtulo kodi, kapena guwa la nsembe limene liyeretsa mtulowo?

20 Chifukwa chake wakulumbira kutchula guwa la nsembe, alumbira limenelo ndi zonse za pamwamba pake.

21 Ndipo wakulumbira kutchula Kachisi, alumbira ameneyo ndi Iye wakukhala momwemo.

22 Ndipo wakulumbira kutchula Kumwamba, alumbira chimpando cha Mulungu, ndi Iye wakukhala pomwepo.

23 Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! Chifukwa mupereka limodzi la magawo khumi la timbeu tonunkhira, ndi katsabola, ndi la chitowe, nimusiya zolemera za chilamulo, ndizo kuweruza kolungama, ndi kuchitira chifundo, ndi chikhulupiriro; koma zijazo munayenera kuzichita, osasiya izi zomwe.

24 Atsogoleri akhungu inu, akukuntha udzudzu, koma mumezangamira.

25 Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! Chifukwa mutsuka kunja kwake kwa chikho ndi mbale, koma m’katimo iwo adzala ndi kulanda ndi kusadziletsa.

26 Mfarisi iwe wakhungu, yambawatsuka m’kati mwa chikho ndi mbale, kuti kunja kwake kukhalenso koyera.

27 Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! Chifukwa mufanafana ndi manda opaka njereza, amene aonekera okoma kunja kwake, koma adzala m’katimo ndi mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zonse.

28 Chomwecho inunso muonekera olungama pamaso pa anthu, koma m’kati muli odzala ndi chinyengo ndi kusaweruzika.

29 Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! Chifukwa mumanga nyumba za pa manda a aneneri, ndipo mukonza manda a anthu olungama,

30 ndi kuti, Ife tikadakhala m’masiku a makolo anthu, sitikadakhala oyanjana nao pa mwazi wa aneneri.

31 Pomwepo mutsimikiza nokha, kuti muli ana a iwo amene anapha aneneri.

32 Dzazani inu muyeso wa makolo anu.

33 Njoka inu, obadwa inu a mamba, mudzatha bwanji kuthawa kulanga kwake kwa Gehena?

34 Chifukwa cha icho, onani, ndituma kwa inu aneneri ndi anzeru ndi alembi; ena a iwo mudzawapha, mudzawapachika; ndi ena a iwo mudzawakwapula m’masunagoge mwanu, ndi kuwazunza, kuchokera kumudzi umodzi, kufikira kumudzi wina;

35 kotero kuti udzafika pa inu mwazi wonse wotayidwa padziko lapansi, kuyambira kumwazi wa Abele wolungamayo, kufikira kumwazi wa Zekariya mwana wa Barakiya, amene munamupha pakati pa Kachisi ndi guwa la nsembe.

36 Indetu ndinena kwa inu, Zinthu zonse izi zidzafika pa mbadwo uwu wamakono.

37 Ha,Yerusalemu, Yerusalemu, amene umapha aneneri, ndi kuwaponya miyala iwo otumidwa kwa iwe! Ine ndinafuna kangati kusonkhanitsa pamodzi ana ako, inde monga thadzi lisonkhanitsa anapiye ake m’mapiko ake, koma inu simunafune ai!

38 Onani, nyumba yanu yasiyidwa kwa inu yabwinja.

39 Pakuti ndinena kwa inu, Simudzandionanso Ine, kuyambira tsopano, kufikira mudzanena,

Wolemekezedwa Iye amene akudza m’dzina la Ambuye.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAT/23-8066f2fba357947549ab68c0f85291c2.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *