Categories
MATEYU

MATEYU 16

Afarisi ndi Asaduki afuna chizindikiro

1 NdipoAfarisindiAsadukianadza, namuyesa, namfunsa Iye awaonetse chizindikiro cha Kumwamba.

2 Koma Iye anayankha, nati kwa iwo, Madzulo munena, Kudzakhala ngwee; popeza thambo lili lacheza.

3 Ndipo m’mawa, Lero nkwa mphepo: popeza thambo lili la cheza chodera. Mudziwa kuzindikira za pa nkhope ya thambo; koma zizindikiro za nyengo ino, simungathe kuzindikira.

4 Obadwa oipa ndi achigololo afunafuna chizindikiro; ndipo sadzalandira chizindikiro china, koma chizindikiro cha Yona. Ndipo Iye anawasiya, nachokapo.

5 Ndipoophunziraanadza kutsidya linalo, naiwala kutenga mikate.

6 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Yang’anirani mupewe chotupitsa mkate cha Afarisi ndi Asaduki.

7 Ndipo iwo anafunsana wina ndi mnzake, nati, Sitinatenge mikate.

8 Koma Yesu, m’mene anadziwa, anati, Ha, inu okhulupirira pang’ono, mufunsana chifukwa ninji wina ndi mnzake, kuti simunatenga mikate?

9 Kodi chikhalire simudziwa, ndipo simukumbukira mikate isanu ija ya anthu aja zikwi zisanu, ndi madengu angati munawatola?

10 Penanso mikate isanu ndi iwiri ija ya anthu zikwi zinai, ndi madengu angati munawatola?

11 Bwanji nanga simudziwa kuti sindinanena kwa inu za mikate? Koma pewani chotupitsa cha Afarisi ndi Asaduki.

12 Pomwepo anadziwitsa kuti sanawauze kupeza chotupitsa cha mikate, koma chiphunzitso cha Afarisi ndi Asaduki.

Chivomerezo cha Petro

13 Ndipo Yesu, pamene anadza ku dziko la ku Kesareya-Filipi, anafunsa ophunzira ake, kuti, Anthu anena kutiMwana wa Munthundiye yani?

14 Ndipo iwo anati, Ena ati, Yohane Mbatizi; koma ena, Eliya; ndipo enanso Yeremiya, kapena mmodzi wa aneneri.

15 Iye ananena kwa iwo, Koma inu mutani kuti Ine ndine yani?

16 Ndipo Simoni Petro anayankha nati, Inu ndinuKhristu, Mwana wa Mulungu wamoyo.

17 Ndipo Yesu anayankha iye, nati, Ndiwe wodala, Simoni Bara-Yona: pakuti thupi ndi mwazi sizinakuululire ichi, koma Atate wanga wa Kumwamba.

18 Ndiponso Ine ndinena kwa iwe, kuti iwe ndiwe Petro, ndipo pa thanthwe ili ndidzakhazikaMpingowanga; ndipo makomo a dziko la akufa sadzagonjetsa uwo.

19 Ndidzakupatsa mafungulo a Ufumu wa Kumwamba; ndipo chimene ukamanga padziko lapansi chidzakhala chomangidwa Kumwamba: ndipo chimene ukachimasula padziko lapansi, chidzakhala chomasulidwa Kumwamba.

20 Pamenepo analamulira ophunzira kuti asauze munthu kuti Iye ndiye Khristu.

21 Kuyambira pamenepo Yesu anayamba kuwalangiza ophunzira ake, kuti kuyenera Iye amuke kuYerusalemu, kukazunzidwa zambiri ndi akulu, ndi ansembe aakulu, ndi alembi; ndi kukaphedwa, ndi tsiku lachitatu kuuka kwa akufa.

22 Ndipo Petro anamtenga Iye, nayamba kumdzudzula, kuti, Dzichitireni chifundo, Ambuye; sichidzatero kwa Inu ai.

23 Koma Iye anapotoloka, nati kwa Petro, Pita kumbuyo kwanga,Satanaiwe; ndiwe chondikhumudwitsa Ine; chifukwa sumasamalira za Mulungu, koma za anthu.

Za kusenza mtanda wake

24 Pomwepo Yesu anati kwa ophunzira ake, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikane yekha, natenge mtanda wake, nanditsate Ine.

25 Pakuti iye amene afuna kupulumutsa moyo wake adzautaya: koma iye amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine, adzaupeza.

26 Pakuti munthu adzapindulanji, akalandira dziko lonse, nataya moyo wake? Kapena munthu adzaperekanji chosintha ndi moyo wake?

27 Pakuti Mwana wa Munthu adzabwera mu ulemerero wa Atate wake, pamodzi ndiangeloake; ndipo pomwepo Iye adzabwezera kwa anthu onse monga machitidwe ao.

28 Indetu ndinena kwa inu, kuti alipo ena a iwo aima pano sadzalawa ndithu imfa, kufikira adzaona Mwana wa Munthu atadza mu ufumu wake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAT/16-39483d6034dad44f37928c6e43b1f582.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *