Categories
MASALIMO

MASALIMO 99

Mulungu wamkulu wachifundo alemekezedwe

1 Yehova ndiye mfumu; mitundu ya anthu injenjemere;

Iye akhala pakati paakerubi; dziko lapansi ligwedezeke.

2 Yehova ndiye wamkulu muZiyoni;

ndipo akwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.

3 Alemekeze dzina lanu lalikulu ndi loopsa.

Ili ndilo loyera.

4 Ndipo mphamvu ya mfumu ikonda chiweruzo;

Inu mukhazikitsa zolunjika,

muchita chiweruzo ndi chilungamo mu Yakobo.

5 Mkwezeni Yehova Mulungu wathu,

ndipo gwadirani poponderapo mapazi ake:

Iye ndiye Woyera.

6 Mwa ansembe ake muli Mose ndi Aroni,

ndi Samuele mwa iwo akuitanira dzina lake;

anaitana kwa Yehova, ndipo Iye anawayankha.

7 Iye analankhula nao mu mtambo woti njo:

Iwo anasunga mboni zake ndi malembawa anawapatsa.

8 Munawayankha, Yehova Mulungu wathu:

munawakhalira Mulungu wakuwakhululukira,

mungakhale munabwezera chilango pa zochita zao.

9 Mkwezeni Yehova Mulungu wathu,

ndipo gwadirani paphiri lake loyera;

pakuti Yehova Mulungu wathu ndiye woyera.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/99-77e66ae4cdf6bfda694f115ffc645d1e.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *