Categories
MASALIMO

MASALIMO 97

Ulemerero wa ufumu wa Mulungu

1 Yehova achita ufumu; dziko lapansi likondwere;

zisumbu zambiri zikondwerere.

2 Pomzinga pali mitambo ndi mdima;

chilungamo ndi chiweruzo ndizo zolimbitsa

mpando wake wachifumu.

3 Moto umtsogolera,

nupsereza otsutsana naye pozungulirapo.

4 Mphezi zake zinaunikira dziko lokhalamo anthu;

dziko lapansi linaona nilinagwedezeka.

5 Mapiri anasungunuka ngati sera pamaso pa Yehova,

pamaso pa Ambuye wa dziko lonse lapansi.

6 Kumwamba kulalikira chilungamo chake,

ndipo mitundu yonse ya anthu ipenya ulemerero wake.

7 Onse akutumikira fano losema,

akudzitamandira nao mafano, achite manyazi:

Mgwadireni Iye, milungu yonse inu.

8 Ziyonianamva nakondwera,

nasekerera ana aakazi a Yuda;

chifukwa cha maweruzo anu, Yehova.

9 Pakuti Inu, Yehova, ndinu Wam’mwambamwamba padziko lonse lapansi,

ndinu wokwezeka kwakukulu pamwamba pa milungu ina yonse.

10 Inu okonda Yehova, danani nacho choipa:

Iye asunga moyo wa okondedwa ake;

awalanditsa m’manja mwa oipa.

11 Kuunika kufesekera wolungama,

ndi chikondwerero oongoka mtima.

12 Kondwerani mwa Yehova, olungama inu;

ndipo yamikani pokumbukira chiyero chake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/97-6c65878c73f9e757113cb19d347e9fb8.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *