Categories
MASALIMO

MASALIMO 91

Mulungu asungadi wodzipereka kwa Iye

1 Iye amene akhala pansi m’ngaka yake ya Wam’mwambamwamba

adzagonera mu mthunzi wa Wamphamvuyonse.

2 Ndidzati kwa Yehova, Pothawirapo panga ndi linga langa;

Mulungu wanga, amene ndimkhulupirira.

3 Pakuti adzakuonjola kumsampha wa msodzi,

kumliri wosakaza.

4 Adzakufungatira ndi nthenga zake,

ndipo udzathawira kunsi kwa mapiko ake;

choonadi chake ndicho chikopa chotchinjiriza.

5 Sudzaopa choopsa cha usiku,

kapena muvi wopita usana;

6 kapena mliri woyenda mumdima,

kapena chionongeko chakuthera usana.

7 Pambali pako padzagwa chikwi,

ndi zikwi khumi padzanja lamanja lako;

sichidzakuyandikiza iwe.

8 Koma udzapenya ndi maso ako,

nudzaona kubwezera chilango oipa.

9 Popeza udati, Inu Yehova, ndinu pothawirapo panga!

Udaika Wam’mwambamwamba chokhalamo chako;

10 palibe choipa chidzakugwera,

ndipo cholanga sichidzayandikiza hema wako.

11 Pakuti adzalamuliraangeloake za iwe,

akusunge m’njira zako zonse.

12 Adzakunyamula pa manja ao,

ungagunde phazi lako pamwala.

13 Udzaponda mkango ndi mphiri;

udzapondereza msona wa mkango ndi chinjoka.

14 Popeza andikondadi ndidzampulumutsa;

ndidzamkweza m’mwamba, popeza adziwa dzina langa.

15 Adzandifuulira Ine ndipo ndidzamyankha;

kunsautso ndidzakhala naye pamodzi;

ndidzamlanditsa, ndi kumchitira ulemu.

16 Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri,

ndi kumuonetsera chipulumutso changa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/91-f6c6a65bedf2646c3fe08f32811e404e.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *