Amitundu apangana kuononga Aisraele. Apempha Mulungu awalanditse
Nyimbo. Salimo la Asafu.
1 Mulungu musakhale chete;
musakhale duu, osanena kanthu, Mulungu.
2 Pakuti taonani, adani anu apokosera,
ndipo okwiyira Inu aweramutsa mutu.
3 Apangana mochenjerera pa anthu anu,
nakhalira upo pa obisika anu.
4 Amati, Tiyeni tiwaononge asakhalenso mtundu wa anthu;
ndipo dzina la Israele lisakumbukikenso.
5 Pakuti anakhalira upo ndi mtima umodzi;
anachitachipanganocha pa Inu.
6 Mahema a Edomu ndi a Aismaele;
Mowabu ndi Ahagiri;
7 Gebala ndi Amoni ndi Amaleke;
Filistiya, pamodzi ndi iwo okhala mu Tiro.
8 Asiriya anaphatikana nao;
anakhala dzanja la ana a Loti.
9 Muwachitire monga munachitira Midiyani;
ndi Sisera, ndi Yabini kumtsinje wa Kisoni,
10 amene anaonongeka ku Endori;
anakhala ngati ndowe ya kumunda.
11 Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu;
mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna,
12 amene anati, Tilande malo okhalamo Mulungu, akhale athu.
13 Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;
ngati ziputu zomka ndi mphepo.
14 Monga moto upsereza nkhalango,
ndi monga lawi liyatsa mapiri.
15 Momwemo muwatsate ndi namondwe,
nimuwaopse ndi kamvulumvulu wanu.
16 Achititseni manyazi pankhope pao;
kuti afune dzina lanu, Yehova.
17 Achite manyazi, naopsedwe kosatha;
ndipo asokonezeke, naonongeke.
18 Kuti adziwe kuti inu nokha, dzina lanu ndinu Yehova,
ndinu Wam’mwambamwamba padziko lonse lapansi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/83-d2cdb0eba6aa3310d96e8863b2c3cdf6.mp3?version_id=1068—