Categories
MASALIMO

MASALIMO 8

Davide aimbira ulemerero wa Mulungu, ndi ulemu umene Mulungu achitira mtundu wa anthu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Gititi. Salimo la Davide.

1 Yehova, Ambuye wathu,

dzina lanu liposadi nanga padziko lonse lapansi!

Inu amene munaika ulemerero wanu pa thambo la kumwamba.

2 M’kamwa mwa makanda ndi oyamwa munakhazikitsa mphamvu,

chifukwa cha otsutsana ndi Inu,

kuti muwaletse mdani ndi wobwezera chilango.

3 Pakuona ine thambo la kumwamba lanu, ntchito ya zala zanu,

mwezi ndi nyenyezi, zimene munazikhazika,

4 munthu ndani kuti mumkumbukira?

Ndi mwana wa munthu kuti mucheza naye?

5 Pakuti munamchepsa pang’ono ndi Mulungu,

munamveka iye korona wa ulemerero ndi ulemu.

6 Munamchititsa ufumu pa ntchito za manja anu;

mudagonjetsa zonse pansi pa mapazi ake;

7 nkhosa ndi ng’ombe, zonsezo,

ndi nyama zakuthengo zomwe;

8 mbalame za m’mlengalenga, ndi nsomba za m’nyanja.

Zopita m’njira za m’nyanja.

9 Yehova, Ambuye wathu,

dzina lanu liposadi nanga padziko lonse lapansi!

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/8-827fd393f5e57445a7dc0fb268d8e7a4.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *