Davide aimbira ulemerero wa Mulungu, ndi ulemu umene Mulungu achitira mtundu wa anthu
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Gititi. Salimo la Davide.
1 Yehova, Ambuye wathu,
dzina lanu liposadi nanga padziko lonse lapansi!
Inu amene munaika ulemerero wanu pa thambo la kumwamba.
2 M’kamwa mwa makanda ndi oyamwa munakhazikitsa mphamvu,
chifukwa cha otsutsana ndi Inu,
kuti muwaletse mdani ndi wobwezera chilango.
3 Pakuona ine thambo la kumwamba lanu, ntchito ya zala zanu,
mwezi ndi nyenyezi, zimene munazikhazika,
4 munthu ndani kuti mumkumbukira?
Ndi mwana wa munthu kuti mucheza naye?
5 Pakuti munamchepsa pang’ono ndi Mulungu,
munamveka iye korona wa ulemerero ndi ulemu.
6 Munamchititsa ufumu pa ntchito za manja anu;
mudagonjetsa zonse pansi pa mapazi ake;
7 nkhosa ndi ng’ombe, zonsezo,
ndi nyama zakuthengo zomwe;
8 mbalame za m’mlengalenga, ndi nsomba za m’nyanja.
Zopita m’njira za m’nyanja.
9 Yehova, Ambuye wathu,
dzina lanu liposadi nanga padziko lonse lapansi!
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/8-827fd393f5e57445a7dc0fb268d8e7a4.mp3?version_id=1068—