Achita nkhawa pokumbuka zochita Mulungu, koma alimbika mtima pokumbuka zina adazichita Iye
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Yedutuni. Salimo la Asafu.
1 Ndidzafuulira kwa Mulungu ndi mau anga;
kwa Mulungu ndi mau anga, ndipo adzanditcherezera khutu.
2 Tsiku la nsautso yanga ndinafuna Ambuye.
Dzanja langa linatambalika usiku, losaleka;
mtima wanga unakana kutonthozedwa.
3 Ndikumbukira Mulungu ndipo ndivutika;
ndilingalira ndipo mzimu wanga ukomoka.
4 Mundikhalitsa maso;
ndigwidwa mtima wosanena kanthu.
5 Ndinaganizira masiku akale,
zaka zakalekale.
6 Ndikumbukira nyimbo yanga usiku;
ndilingalira mumtima mwanga;
mzimu wanga unasanthula.
7 Kodi Ambuye adzataya nthawi yonse?
Osabwerezanso kukondwera nafe.
8 Chifundo chake chalekeka konsekonse kodi?
Lonjezano lake lidatha kodi ku mibadwo yonse?
9 Kodi Mulungu waiwala kuchita chifundo?
Watsekereza kodi nsoni zokoma zake mumkwiyo?
10 Ndipo ndinati, Chindiwawa ichi;
koma ndikumbukira zaka za dzanja lamanja la Wam’mwambamwamba.
11 Ndidzakumbukira zimene adazichita Yehova;
inde, ndidzakumbukira zodabwitsa zanu zoyambira kale.
12 Ndipo ndidzalingalira ntchito yanu yonse,
ndi kulingalirabe zimene munazichita Inu.
13 Mulungu, m’malo opatulika muli njira yanu;
Mulungu wamkulu ndani monga Mulungu?
14 Inu ndinu Mulungu wakuchita chodabwitsa;
munazindikiritsa mphamvu yanu mwa mitundu ya anthu.
15 Munaombola anthu anu ndi mkono wanu,
ndiwo ana a Yakobo, ndi a Yosefe.
16 Madziwo anakuonani Mulungu;
anakuonani madziwo; anachita mantha,
zozama zomwe zinanjenjemera.
17 Makongwa anatsanula madzi;
thambo lidamvetsa liu lake;
mivi yanu yomwe inatulukira.
18 Liu la bingu lanu linatengezanatengezana;
mphezi zinaunikira ponse pali anthu;
dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 Njira yanu inali m’nyanja,
koyenda Inu nkumadzi aakulu,
ndipo mapazi anu sanadziwike.
20 Munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa,
ndi dzanja la Mose ndi Aroni.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/77-d06cca7a2d01417e2d34d1e031c85145.mp3?version_id=1068—