Ulemerero ndi mphamvu ya Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Salimo la Asafu. Nyimbo.
1 Mulungu adziwika mwa Yuda,
dzina lake limveka mwa Israele.
2 Msasa wake unali mu Salemu,
ndipo pokhala Iye muZiyoni.
3 Pomwepo anathyola mivi ya pauta;
chikopa, ndi lupanga, ndi nkhondo.
4 Inu ndinu wakuunikira, ndi womveka
wakuposa mapiri muli achifwamba.
5 Olimba mtima chifunkhidwa chuma chao, agona tulo tao;
amuna onse amphamvu asowa manja ao.
6 Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo,
galeta ndi kavalo yemwe anagwa m’tulo.
7 Inu ndinu woopsa;
ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala chilili ndani pamaso panu?
8 Mudamveketsa chiweruzo chochokera Kumwamba;
dziko lapansi linachita mantha, nilinakhala chete,
9 pakuuka Mulungu kuti aweruze,
kuti apulumutse ofatsa onse a padziko lapansi.
10 Indedi, kuzaza kwake kwa munthu kudzakulemekezani;
chotsalira cha kuzazaku mudzachiletsa.
11 Windani ndipo chitirani Yehova Mulungu wanu zowindazo;
onse akumzinga abwere nacho chopereka
cha kwa Iye amene ayenera kumuopa.
12 Iye adzadula mzimu wa akulu;
akhala woopsa kwa mafumu a padziko lapansi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/76-6d49cd8d3a95a8d09509157e28fcb6e7.mp3?version_id=1068—