Categories
MASALIMO

MASALIMO 75

Mulungu woweruza asiyanitsa pakati pa odzikuza ndi olungama

Kwa Mkulu wa Nyimbo: Altasyeti. Salimo la Asafu. Nyimbo.

1 Tikuyamikani Inu, Mulungu;

tiyamika, pakuti dzina lanu lili pafupi;

afotokozera zodabwitsa zanu.

2 Pakuona nyengo yake ndidzaweruza molunjika.

3 Lasungunuka dziko lapansi, ndi onse okhalamo;

ndinachirika mizati yake.

4 Ndinati kwa odzitamandira,

musamachita zodzitamandira;

ndi kwa oipa, Musamakweza nyanga;

5 musamakwezetsa nyanga yanu;

musamalankhula ndi khosi louma.

6 Pakuti kukuzaku sikuchokera kum’mawa,

kapena kumadzulo, kapena kuchipululu.

7 Pakuti Mulungu ndiye woweruza;

achepsa wina, nakuza wina.

8 Pakuti m’dzanja la Yehova muli chikho;

ndi vinyo wake achita thovu;

chidzala ndi zosakanizira, ndipo atsanulako.

Indedi, oipa onse a padziko lapansi adzamwa

nadzagugudiza nsenga zake.

9 Koma ine ndidzalalikira kosalekeza,

ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wa Yakobo.

10 Ndipo ndidzatseteka nyanga zonse za oipa;

koma nyanga za wolungama zidzakwezeka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/75-52b7b03dd59f18d15cd25d480b6410d9.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *