Categories
MASALIMO

MASALIMO 70

Davide apempha Mulungu amlanditse msanga

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide, la chikumbutso.

1 Fulumirani kundipulumutsa, Mulungu!

Fulumirani kundithandiza, Yehova.

2 Achite manyazi, nadodome

amene afuna moyo wanga.

Abwezedwe m’mbuyo, napepulidwe

amene akonda kundichitira choipa.

3 Abwerere, kukhale mphotho ya manyazi ao

amene akuti, Hede, hede.

4 Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu;

nanene kosalekeza iwo akukonda chipulumutso chanu,

abuke Mulungu.

5 Koma ine ndine wozunzika ndi waumphawi;

mundifulumirire, Mulungu.

Inu ndinu mthandizi wanga ndi Mpulumutsi wanga;

musachedwe, Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/70-251047a461c8e820f60f8ead5989c355.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *