Amitundu alemekeze Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo, pa Neginoto. Salimo. Nyimbo.
1 Atichitire chifundo Mulungu, ndi kutidalitsa,
atiwalitsire nkhope yake;
2 kuti njira yanu idziwike padziko lapansi,
chipulumutso chanu mwaamitunduonse.
3 Anthu akuyamikeni, Mulungu;
anthu onse akuyamikeni.
4 Anthu akondwere, nafuule mokondwera;
pakuti mudzaweruza anthu molunjika,
ndipo mudzalangiza anthu padziko lapansi.
5 Anthu akuyamikeni, Mulungu;
anthu onse akuyamikeni.
6 Dziko lapansi lapereka zipatso zake,
Mulungu, Mulungu wathu adzatidalitsa.
7 Mulungu adzatidalitsa;
ndipo malekezero onse a dziko lapansi adzamuopa Iye.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/67-029d8e9e029b86de068d98b51bdff7f7.mp3?version_id=1068—