Categories
MASALIMO

MASALIMO 67

Amitundu alemekeze Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo, pa Neginoto. Salimo. Nyimbo.

1 Atichitire chifundo Mulungu, ndi kutidalitsa,

atiwalitsire nkhope yake;

2 kuti njira yanu idziwike padziko lapansi,

chipulumutso chanu mwaamitunduonse.

3 Anthu akuyamikeni, Mulungu;

anthu onse akuyamikeni.

4 Anthu akondwere, nafuule mokondwera;

pakuti mudzaweruza anthu molunjika,

ndipo mudzalangiza anthu padziko lapansi.

5 Anthu akuyamikeni, Mulungu;

anthu onse akuyamikeni.

6 Dziko lapansi lapereka zipatso zake,

Mulungu, Mulungu wathu adzatidalitsa.

7 Mulungu adzatidalitsa;

ndipo malekezero onse a dziko lapansi adzamuopa Iye.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/67-029d8e9e029b86de068d98b51bdff7f7.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *