Categories
MASALIMO

MASALIMO 65

Davide alemekeza Mulungu pa madalitso ochuluka

Kwa Mkulu wa Nyimbo: Salimo la Davide. Nyimbo.

1 MuZiyoniakulemekezani Inu mwachete, Mulungu,

adzakuchitirani Inu chowindachi.

2 Wakumva pemphero Inu,

zamoyo zonse zidzadza kwa Inu.

3 Mphulupulu zinandipambana;

koma mudzafafaniza zolakwa zathu.

4 Wodala munthuyo mumsankha, ndi kumyandikizitsa,

akhale m’mabwalo anu.

Tidzakhuta nazo zokoma za m’nyumba yanu,

za m’malo oyera a Kachisi wanu.

5 Mudzatiyankha nazo zoopsa m’chilungamo,

Mulungu wa chipulumutso chathu;

ndinu chikhulupiriko cha malekezero onse a dziko lapansi,

ndi cha iwo okhala kutali kunyanja.

6 Ndinu amene mukhazikitsa mapiri ndi mphamvu yanu;

pozingidwa nacho chilimbiko.

7 Amene atontholetsa kukuntha kwa nyanja,

kukuntha kwa mafunde ake,

ndi phokoso la mitundu ya anthu.

8 Ndipo iwo akukhala kumalekezero adzachita mantha

chifukwa cha zizindikiro zanu;

mukondweretsa apo patulukira dzuwa, ndi apo lilowera.

9 Mucheza nalo dziko lapansi, mulithirira,

mulilemeretsa kwambiri;

mtsinje wa Mulungu udzala nao madzi,

muwameretsera tirigu m’mene munakonzera nthaka.

10 Mukhutitsa nthaka yake yolima;

mufafaniza nthumbira zake;

muiolowetsa ndi mvumbi;

mudalitsa mmera wake.

11 Muveka chakachi ndi ukoma wanu;

ndipo mabande anu akukha zakucha.

12 Akukha pa mabusa a m’chipululu;

ndipo mapiri azingika nacho chimwemwe.

13 Podyetsa mpodzaza ndi zoweta;

ndipo zigwa zakutidwa ndi tirigu;

zifuula mokondwera, inde ziimbira.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/65-b7355099f446294b6dd7e354ffe4751b.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *