Categories
MASALIMO

MASALIMO 61

Poopsedwa Davide athamangira Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Salimo la Davide.

1 Imvani mfuu wanga, Mulungu;

mverani pemphero langa.

2 Ku malekezero a dziko lapansi ndidzafuulira kwa Inu,

pomizika mtima wanga.

Nditsogolereni kuthanthwe londiposa ine m’kutalika kwake.

3 Pakuti munakhala pothawirapo panga;

nsanja yolimba pothawa mdani ine.

4 Ndidzagoneragonerabe m’chihema mwanu;

ndidzathawira mobisalamo m’mapiko anu.

5 Pakuti Inu, Mulungu, mudamva zowinda zanga;

munandipatsa cholowa cha iwo akuopa dzina lanu.

6 Mudzatalikitsa moyo wa mfumu.

Zaka zake zidzafikira mibadwomibadwo.

7 Adzakhala nthawi zonse pamaso pa Mulungu;

mumpatse chifundo ndi choonadi zimsunge.

8 Potero ndidzaimba zolemekeza dzina lanu kunthawi zonse,

kuti ndichite zowinda zanga tsiku ndi tsiku.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/61-1e56a0cd41ef1a4cbbcc64d8486c8292.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *