Categories
MASALIMO

MASALIMO 6

Davide apempha chifundo kwa Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto, pa Seminiti. Salimo la Davide.

1 Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu,

ndipo musandilange muukali wanu.

2 Mundichitire chifundo, Yehova; pakuti ndalefuka ine.

Mundichize, Yehova; pakuti anthunthumira mafupa anga.

3 Moyo wanganso wanthunthumira kwakukulu;

ndipo Inu, Yehova, kufikira liti?

4 Bwererani Yehova, landitsani moyo wanga;

ndipulumutseni chifukwa cha kukoma mtima kwanu.

5 Pakuti muimfa m’mosakumbukira Inu;

m’mandamo adzakuyamikani ndani?

6 Ndalema nako kuusa moyo kwanga;

ndiyandamitsa kama wanga usiku wonse;

mphasa yanga ndiolobza ndi misozi yanga.

7 Lapuwala diso langa chifukwa cha chisoni;

lakalamba chifukwa cha onse akundisautsa.

8 Chokani kwa ine, nonsenu akuchita zopanda pake;

pakuti wamva Yehova mau a kulira kwanga.

9 Wamva Yehova kupemba kwanga;

Yehova adzalandira pemphero langa.

10 Adzachita manyazi, nadzanthunthumira kwakukulu

adani anga onse;

adzabwerera, nadzachita manyazi modzidzimuka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/6-12e6ac2c0a2d65440fbb65d805f91b7a.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *