Categories
MASALIMO

MASALIMO 59

Davide apempha Mulungu amlanditse, nadzinenera wosalakwa

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Altasheti. Mikitamu wa Davide; muja Saulo anatuma anthu adikire nyumba yake, kuti amuphe.

1 Ndilanditseni kwa adani anga, Mulungu wanga,

ndiikeni pamsanje kwa iwo akundiukira.

2 Mundilanditse kwa ochita zopanda pake,

ndipo ndipulumutseni kwa anthu olira mwazi.

3 Pakuti onani, alalira moyo wanga;

amphamvu andipangira chiwembu,

osachimwa, osalakwa ine, Yehova,

4 osawapatsa chifukwa ine, athamanga nadzikonza.

Galamukani kukomana nane, ndipo penyani.

5 Ndinu Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Israele.

Ukani kukazondaamitunduonse,

musachitire chifundo mmodzi yense

wakuchita zopanda pake monyenga.

6 Abwera madzulo, auwa ngati galu,

nazungulira mzinda.

7 Onani abwetuka pakamwa pao;

m’milomo mwao muli lupanga,

pakuti amati, Amva ndani?

8 Koma Inu, Yehova, mudzawaseka;

mudzalalatira amitundu onse.

9 Inu, mphamvu yanga, ndidzakulindirani;

pakuti Mulungu ndiye msanje wanga.

10 Mulungu wa chifundo changa adzandichingamira,

adzandionetsa tsoka la adani anga.

11 Musawapheretu, angaiwale anthu anga,

muwabalalitse mwa mphamvu yanu, ndipo muwagwetse,

Ambuye, ndinu chikopa chathu.

12 Pakamwa pao achimwa ndi mau onse a pa milomo yao,

potero akodwe m’kudzitamandira kwao,

ndiponso chifukwa cha kutemberera ndi bodza azilankhula.

13 Muwathe mumkwiyo, muwagulule psiti.

Ndipo adziwe kuti Mulungu ndiye woweruza mu Yakobo,

kufikira malekezero a dziko la pansi.

14 Ndipo abwere madzulo, auwe ngati galu,

nazungulire mzinda.

15 Ayendeyende ndi kufuna chakudya,

nachezere osakhuta.

16 Koma ine, ndidzaimbira mphamvu yanu;

inde ndidzaimbitsa chifundo chanu mamawa,

pakuti Inu mwakhala msanje wanga,

ndi pothawirapo ine tsiku la nsautso yanga.

17 Ndidzaimbira zakukulemekezani Inu, mphamvu yanga;

pakuti Mulungu ndiye msanje wanga,

Mulungu wa chifundo changa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/59-e89d78b60b007ab882f1c5c2366da500.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *