Categories
MASALIMO

MASALIMO 58

Davide adzudzula oipa Mulungu awalange

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Altasyeti. Mikitamu wa Davide.

1 Kodi muli chete ndithu poyenera inu kunena zolungama?

Muweruza ana anthu molunjika kodi?

2 Inde, mumtima muchita zosalungama;

padziko lapansi mugawira anthu chiwawa cha m’manja mwanu.

3 Oipa achita chilendo chibadwire,

asokera kuyambira kubadwa kwao, nanena bodza.

4 Ululu wao ukunga wa njoka;

akunga mphiri yogontha m’khutu, itseka m’khutu mwake.

5 Imene siimvera liu la oitana,

akuchita matsenga mochenjeratu.

6 Thyolani mano ao m’kamwa mwao, Mulungu,

zulani zitsakano za misona ya mkango, Yehova.

7 Apitetu ngati madzi oyenda;

popiringidza mivi yake ikhale yodukaduka.

8 Apite ngati nkhono yosungunuka;

asaone dzuwa monga mtayo.

9 Miphika yanu isanagwire moto waminga,

adzaiuluza, yaiwisi ndi yoyaka.

10 Wolungama adzakondwera pakuona kubwezera chilango,

adzasamba mapazi ake m’mwazi wa woipa.

11 Ndipo anthu adzati, Indedi, pali mphotho kwa wolungama.

Indedi, pali Mulungu wakuweruza padziko lapansi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/58-b824fc7f69079b8cbb5de62ba641a2a6.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *