Davide apempha Mulungu amtchinjirize, namlemekezapo
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Altasheti. Mikitamu wa Davide; muja anathawa Saulo, ali m’phanga.
1 Mundichitire chifundo, Mulungu, mundichitire chifundo;
pakuti moyo wanga ukhulupirira Inu,
ndipo ndithawira kumthunzi wa mapiko anu,
kufikira zosakazazo zidzapita.
2 Ndidzafuulira kwa Mulungu Wam’mwambamwamba;
ndiye Mulungu wonditsirizira zonse.
3 Adzanditumizira m’mwamba, nadzandipulumutsa
ponditonza wofuna kundimeza;
Mulungu adzatumiza chifundo chake ndi choonadi chake.
4 Moyo wanga uli pakati pa mikango;
ndigona pakati pa oyaka moto,
ndiwo ana a anthu amene mano ao ali nthungo ndi mivi,
ndipo lilime lao ndilo lupanga lakuthwa.
5 Mukwezeke m’mwambamwamba, Mulungu;
ulemerero wanu ukhale pamwamba padziko lonse lapansi.
6 Ananditchera ukonde apo ndiyenda;
moyo wanga wawerama.
Anandikumbira mbuna patsogolo panga;
anagwa m’kati mwake iwo okha.
7 Mtima wanga wakhazikika, Mulungu, ndakhazika mtima;
ndidzaimba, inde, ndidzaimba zolemekeza.
8 Galamuka, ulemu wanga; galamukani chisakasa ndi zeze!
Ndidzauka ndekha mamawa.
9 Ndidzakuyamikirani mwa anthu, Ambuye,
ndidzakuimbirani mwa mitundu.
10 Pakuti chifundo chanu nchachikulu kufikira m’mwamba,
ndi choonadi chanu kufikira mitambo.
11 Kwezekani m’mwambamwamba, Mulungu;
ulemerero wanu ukhale pamwamba m’dziko lonse lapansi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/57-b8e32b44aecaea2420ecc0fbf388b73f.mp3?version_id=1068—