Davide apempha Mulungu amlanditse
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Chilangizo cha Davide. Muja Azifi anamuka nauza Saulo, kuti, Kodi Davide sabisala kwathu nanga?
1 Ndipulumutseni, Mulungu, mwa dzina lanu,
ndipo mundiweruze ndi mphamvu yanu.
2 Imvani pemphero langa, Mulungu;
tcherani khutu mau a pakamwa panga.
3 Pakuti alendo andiukira,
ndipo oopsa afunafuna moyo wanga;
sadziikira Mulungu pamaso pao.
4 Taonani, Mulungu ndiye mthandizi wanga,
Ambuye ndiye wachirikiza moyo wanga.
5 Adzabwezera choipa adani anga,
aduleni m’choonadi chanu.
6 Ine mwini ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu,
ndidzayamika dzina lanu, Yehova, pakuti nlokoma.
7 Pakuti anandilanditsa m’nsautso yonse;
ndipo ndapenya ndi diso langa icho ndakhumbira pa adani anga.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/54-7e0db2663d17ad9db483aea5e9664885.mp3?version_id=1068—