Categories
MASALIMO

MASALIMO 53

Kupusa ndi kuipa kwa anthu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Mahalati. Chilangizo cha Davide.

1 Chitsiru chimati mumtima mwake, Kulibe Mulungu.

Achita zovunda, achita chosalungama chonyansa;

kulibe wakuchita bwino.

2 Mulungu m’mwamba anaweramira pa ana a anthu,

kuti aone ngati aliko wanzeru,

wakufuna Mulungu.

3 Onse anabwerera; anavunda mtima pamodzi;

palibe mmodzi wakuchita bwino, nnena mmodzi.

4 Kodi ochita zopanda pake sadziwa?

Pomadya anthu anga monga akudya mkate;

ndipo saitana Mulungu.

5 Pamenepo anaopa kwakukulu, popanda chifukwa cha kuopa,

pakuti Mulungu anamwaza mafupa a iwo akuzinga iwe;

unawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawakaniza.

6 Ha, chipulumutso cha Israele chichokere muZiyoni!

Pakubweretsa Mulungu anthu ake a m’ndende,

Yakobo adzakondwera, Israele adzasekera.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/53-f695e745f1b28f07ca0f2bd5d9677d56.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *