Kupusa ndi kuipa kwa anthu
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Mahalati. Chilangizo cha Davide.
1 Chitsiru chimati mumtima mwake, Kulibe Mulungu.
Achita zovunda, achita chosalungama chonyansa;
kulibe wakuchita bwino.
2 Mulungu m’mwamba anaweramira pa ana a anthu,
kuti aone ngati aliko wanzeru,
wakufuna Mulungu.
3 Onse anabwerera; anavunda mtima pamodzi;
palibe mmodzi wakuchita bwino, nnena mmodzi.
4 Kodi ochita zopanda pake sadziwa?
Pomadya anthu anga monga akudya mkate;
ndipo saitana Mulungu.
5 Pamenepo anaopa kwakukulu, popanda chifukwa cha kuopa,
pakuti Mulungu anamwaza mafupa a iwo akuzinga iwe;
unawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawakaniza.
6 Ha, chipulumutso cha Israele chichokere muZiyoni!
Pakubweretsa Mulungu anthu ake a m’ndende,
Yakobo adzakondwera, Israele adzasekera.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/53-f695e745f1b28f07ca0f2bd5d9677d56.mp3?version_id=1068—