Davide aneneratu za chionongeko cha oipa, iye nakhulupirira Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Chilangizo cha Davide; muja analowa Doegi Mwedomu nauza Saulo nati kwa iye, Davide walowa m’nyumba ya Ahimeleki.
1 Udzitamandiranji ndi choipa, chiphona iwe?
Chifundo cha Mulungu chikhala tsiku lonse.
2 Lilime lako likupanga zoipa;
likunga lumo lakuthwa, lakuchita monyenga.
3 Ukonda choipa koposa chokoma;
ndi bodza koposa kunena chilungamo,
4 ukonda mau onse akuononga,
lilime lachinyengo, iwe.
5 Potero Mulungu adzakupasula kunthawi zonse,
adzakuchotsa nadzakukwatula m’hema mwako,
nadzakuzula, kukuchotsa m’dziko la amoyo.
6 Ndipo olungama adzachiona, nadzaopa,
nadzamseka, ndi kuti,
7 Tapenyani, suyu munthuyu amene sanamuyese Mulungu mphamvu yake;
amene anatama kuchuluka kwa chuma chake,
nadzilimbitsa m’kuipsa kwake.
8 Koma ine ndine ngati mtengo wauwisi waazitona
m’nyumba ya Mulungu.
Ndikhulupirira chifundo cha Mulungu kunthawi za nthawi.
9 Ndidzakuyamikani kosatha, popeza Inu munachichita ichi,
ndipo ndidzayembekeza dzina lanu, pakuti ichi nchokoma,
pamaso pa okondedwa anu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/52-714c69d5d39300a0a025329eac12d0ed.mp3?version_id=1068—