Categories
MASALIMO

MASALIMO 52

Davide aneneratu za chionongeko cha oipa, iye nakhulupirira Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Chilangizo cha Davide; muja analowa Doegi Mwedomu nauza Saulo nati kwa iye, Davide walowa m’nyumba ya Ahimeleki.

1 Udzitamandiranji ndi choipa, chiphona iwe?

Chifundo cha Mulungu chikhala tsiku lonse.

2 Lilime lako likupanga zoipa;

likunga lumo lakuthwa, lakuchita monyenga.

3 Ukonda choipa koposa chokoma;

ndi bodza koposa kunena chilungamo,

4 ukonda mau onse akuononga,

lilime lachinyengo, iwe.

5 Potero Mulungu adzakupasula kunthawi zonse,

adzakuchotsa nadzakukwatula m’hema mwako,

nadzakuzula, kukuchotsa m’dziko la amoyo.

6 Ndipo olungama adzachiona, nadzaopa,

nadzamseka, ndi kuti,

7 Tapenyani, suyu munthuyu amene sanamuyese Mulungu mphamvu yake;

amene anatama kuchuluka kwa chuma chake,

nadzilimbitsa m’kuipsa kwake.

8 Koma ine ndine ngati mtengo wauwisi waazitona

m’nyumba ya Mulungu.

Ndikhulupirira chifundo cha Mulungu kunthawi za nthawi.

9 Ndidzakuyamikani kosatha, popeza Inu munachichita ichi,

ndipo ndidzayembekeza dzina lanu, pakuti ichi nchokoma,

pamaso pa okondedwa anu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/52-714c69d5d39300a0a025329eac12d0ed.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *