Categories
MASALIMO

MASALIMO 51

Davide avomereza kuchimwa kwake, apempha Mulungu amkhululukire, asamchotsere Mzimu Woyera

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide; m’mene anamdzera Natani mneneriyo atalowa iye kwa Bateseba.

1 Mundichitire ine chifundo, Mulungu,

monga mwa kukoma mtima kwanu;

monga mwa unyinji wa nsoni zanu zokoma

mufafanize machimo anga.

2 Mubwereze kunditsuka mphulupulu yanga,

ndipo mundiyeretse kundichotsera choipa changa.

3 Chifukwa ndazindikira machimo anga;

ndipo choipa changa chili pamaso panga chikhalire.

4 Pa Inu, Inu nokha, ndinachimwa,

ndipo ndinachichita choipacho pamaso panu;

kuti mukhale wolungama pakulankhula Inu,

mukhalenso woyera pa kuweruza kwanu.

5 Onani, ndinabadwa m’mphulupulu,

ndipo mai wanga anandilandira m’zoipa.

6 Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m’malo a m’katimo;

ndipo m’malo a m’tseri mudzandidziwitsa nzeru.

7 Mundiyeretse ndihisopendipo ndidzayera;

munditsuke ndipo ndidzakhala wa mbuu woposa matalala.

8 Mundimvetse chimwemwe ndi kusekera,

kuti mafupawo munawathyola akondwere.

9 Muzibisire nkhope yanu zolakwa zanga,

ndipo mufafanize mphulupulu zanga zonse.

10 Mundilengere mtima woyera, Mulungu;

mukonze mzimu wokhazikika m’kati mwanga.

11 Musanditaye kundichotsa pamaso panu;

musandichotsere Mzimu wanu Woyera.

12 Mundibwezere chimwemwe cha chipulumutso chanu;

ndipo mzimu wakulola undigwirizize.

13 Pomwepo ndidzalangiza ochimwa njira zanu;

ndipo olakwa adzabwera kwa Inu.

14 Mundilanditse kumlandu wa mwazi, Mulungu,

ndinu Mulungu wa chipulumutso changa;

lilime langa lidzakweza nyimbo ya chilungamo chanu.

15 Ambuye, tsegulani pa milomo yanga;

ndipo pakamwa panga padzalalikira ulemekezo wanu.

16 Pakuti simukondwera ndi nsembe, mwenzi nditapereka;

nsembe yopsereza simuikonda.

17 Nsembe za Mulungu ndizo mzimu wosweka;

Inu, Mulungu, simudzaupeputsa mtima wosweka ndi wolapa.

18 ChitiraniZiyonichokoma monga mwa kukondwera kwanu;

mumange malinga a miyala aYerusalemu.

19 Pamenepo mudzakondwera nazo nsembe zachilungamo,

ndi nsembe yopsereza ndi yopsereza yathunthu;

pamenepo adzapereka

ng’ombe paguwa lanu la nsembe.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/51-301c95ad4d072dd3013079c69eead3fa.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *