Davide avomereza kuchimwa kwake, apempha Mulungu amkhululukire, asamchotsere Mzimu Woyera
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide; m’mene anamdzera Natani mneneriyo atalowa iye kwa Bateseba.
1 Mundichitire ine chifundo, Mulungu,
monga mwa kukoma mtima kwanu;
monga mwa unyinji wa nsoni zanu zokoma
mufafanize machimo anga.
2 Mubwereze kunditsuka mphulupulu yanga,
ndipo mundiyeretse kundichotsera choipa changa.
3 Chifukwa ndazindikira machimo anga;
ndipo choipa changa chili pamaso panga chikhalire.
4 Pa Inu, Inu nokha, ndinachimwa,
ndipo ndinachichita choipacho pamaso panu;
kuti mukhale wolungama pakulankhula Inu,
mukhalenso woyera pa kuweruza kwanu.
5 Onani, ndinabadwa m’mphulupulu,
ndipo mai wanga anandilandira m’zoipa.
6 Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m’malo a m’katimo;
ndipo m’malo a m’tseri mudzandidziwitsa nzeru.
7 Mundiyeretse ndihisopendipo ndidzayera;
munditsuke ndipo ndidzakhala wa mbuu woposa matalala.
8 Mundimvetse chimwemwe ndi kusekera,
kuti mafupawo munawathyola akondwere.
9 Muzibisire nkhope yanu zolakwa zanga,
ndipo mufafanize mphulupulu zanga zonse.
10 Mundilengere mtima woyera, Mulungu;
mukonze mzimu wokhazikika m’kati mwanga.
11 Musanditaye kundichotsa pamaso panu;
musandichotsere Mzimu wanu Woyera.
12 Mundibwezere chimwemwe cha chipulumutso chanu;
ndipo mzimu wakulola undigwirizize.
13 Pomwepo ndidzalangiza ochimwa njira zanu;
ndipo olakwa adzabwera kwa Inu.
14 Mundilanditse kumlandu wa mwazi, Mulungu,
ndinu Mulungu wa chipulumutso changa;
lilime langa lidzakweza nyimbo ya chilungamo chanu.
15 Ambuye, tsegulani pa milomo yanga;
ndipo pakamwa panga padzalalikira ulemekezo wanu.
16 Pakuti simukondwera ndi nsembe, mwenzi nditapereka;
nsembe yopsereza simuikonda.
17 Nsembe za Mulungu ndizo mzimu wosweka;
Inu, Mulungu, simudzaupeputsa mtima wosweka ndi wolapa.
18 ChitiraniZiyonichokoma monga mwa kukondwera kwanu;
mumange malinga a miyala aYerusalemu.
19 Pamenepo mudzakondwera nazo nsembe zachilungamo,
ndi nsembe yopsereza ndi yopsereza yathunthu;
pamenepo adzapereka
ng’ombe paguwa lanu la nsembe.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/51-301c95ad4d072dd3013079c69eead3fa.mp3?version_id=1068—