Mau a kulemekeza Mulungu mwini dziko lonse lapansi
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la ana a Kora.
1 Ombani m’manja, mitundu yonse ya anthu;
fuulirani kwa Mulungu ndi liu la kuimbitsa.
2 Pakuti Yehova Wam’mwambamwamba ndiye woopsa;
ndiye mfumu yaikulu padziko lonse lapansi.
3 Atigonjetsera anthu,
naikaamitundupansi pa mapazi athu.
4 Atisankhira cholowa chathu,
chokometsetsa cha Yakobo amene anamkonda.
5 Mulungu wakwera ndi mfuu,
Yehova ndi liu la lipenga.
6 Imbirani Mulungu, imbirani;
imbirani mfumu yathu, imbirani.
7 Pakuti Mulungu ndiye mfumu ya dziko lonse lapansi;
imbirani ndi chilangizo.
8 Mulungu ndiye mfumu ya amitundu,
Mulungu akhala pa mpando wachifumu wake woyera.
9 Akulu a anthu asonkhana
akhale anthu a Mulungu wa Abrahamu,
pakuti zikopa za dziko lapansi nza Mulungu;
akwezeka kwakukulu Iyeyo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/47-3f699d23b0b2fdb809c608e8b2a6d8f4.mp3?version_id=1068—