Davide alira akhale ku Kachisi
1 Mundiweruzire, Mulungu, ndipo mundinenere mlandu kwa anthu opanda chifundo.
Mundilanditse kwa munthu wonyenga ndi wosalungama.
2 Pakuti Inu ndinu Mulungu wa mphamvu yanga; mwanditayiranji?
Ndimayenderanji woliralira chifukwa cha kundipsinja mdani?
3 Tumizirani kuunika kwanu ndi choonadi chanu zinditsogolere;
zindifikitse kuphiri lanu loyera,
kumene mukhala Inuko.
4 Kuti ndipite kufikira guwa la nsembe la Mulungu,
kufikira Mulungu wa chimwemwe changa chenicheni,
ndi kuti ndikuyamikeni ndi zeze, Mulungu, Mulungu wanga.
5 Udziweramiranji moyo wanga iwe?
Ndi kuzingwa m’kati mwanga?
Yembekeza Mulungu: pakuti ndidzamyamikanso,
ndiye chipulumutso cha nkhope yanga, ndi Mulungu wanga.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/43-8197488d3ef56fba8d833b7567548e6e.mp3?version_id=1068—