Categories
MASALIMO

MASALIMO 42

Mtima wolira kuyanjana ndi Mulungu mu Kachisi

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Chilangizo cha kwa ana a Kora.

1 Monga nswala ipuma wefuwefu kukhumba mitsinje;

motero moyo wanga upuma wefuwefu kukhumba Inu, Mulungu.

2 Moyo wanga uli ndi ludzu la kwa Mulungu,

la kwa Mulungu wamoyo.

Ndikadze liti kuoneka pamaso pa Mulungu?

3 Misozi yanga yakhala ngati chakudya changa,

usana ndi usiku;

pakunena iwo kwa ine dzuwa lonse,

Mulungu wako ali kuti?

4 Ndidzikumbukira izi ndipo nditsanulira moyo wanga m’kati mwa ine,

pakuti ndinkapita ndi unyinji wa anthu,

ndinawatsogolera kunyumba ya Mulungu,

ndi mau akuimbitsa ndi kuyamika,

ndi unyinji wakusunga dzuwa lokondwera.

5 Udziweramiranji moyo wanga iwe?

Ndi kuzingwa m’kati mwanga?

Yembekeza Mulungu, pakuti ndidzamyamikanso

chifukwa cha chipulumutso cha nkhope yake.

6 Mulungu wanga, moyo wanga

udziweramira m’kati mwanga;

chifukwa chake ndikumbukira Inu m’dziko la Yordani,

ndi mu Aheremoni, m’kaphiri ka Mizara.

7 Madzi akuya aitanizana ndi madzi akuya,

pa mkokomo wa matiti anu;

mafunde onse a nyondonyondo anandimiza ine.

8 Koma usana Yehova adzalamulira chifundo chake,

ndipo usiku nyimbo yake idzakhala ndi ine.

Inde pemphero la kwa Mulungu wa moyo wanga.

9 Ndidzati kwa Mulungu, thanthwe langa,

mwandiiwala chifukwa ninji?

Ndimayenderanji wakulira

chifukwa cha kundipsinja mdaniyo?

10 Adani anga andinyoza ndi kundithyola mafupa anga;

pakunena ndine dzuwa lonse,

Mulungu wako ali kuti?

11 Udziweramiranji moyo wanga iwe?

Ndi kuzingwa m’kati mwanga?

Yembekeza Mulungu; pakuti ndidzamlemekeza tsopanonso,

ndiye chipulumutso cha nkhope yanga ndi Mulungu wanga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/42-ae42dc50afb061e3a3a74ad4c3630ce9.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *