Kupepuka kwa moyo uno
Kwa Mkulu wa Nyimbo, kwa Yedutuni. Salimo la Davide.
1 Ndinati, Ndidzasunga njira zanga,
kuti ndingachimwe ndi lilime langa.
Ndidzasunga pakamwa panga ndi cham’kamwa,
pokhala woipa ali pamaso panga.
2 Ndinatonthola osanena mau,
ndinakhala chete osalawa chokoma;
ndipo chisoni changa chinabuka.
3 Mtima wanga unatentha m’kati mwa ine;
unayaka moto pakulingirira ine.
Pamenepo ndinalankhula ndi lilime langa,
4 Yehova, mundidziwitse chimaliziro changa,
ndi mawerengedwe a masiku anga ndi angati;
ndidziwe malekezero anga.
5 Onani, munaika masiku anga akhale monga kuyesa dzanja;
ndipo zaka zanga zili ngati chabe pamaso panu,
Indedi munthu aliyense angakhale wokhazikika, ali chabe konse.
6 Indedi munthu ayenda ngati mthunzi;
Indedi avutika chabe: Asonkhanitsa chuma,
ndipo sadziwa adzachilandira ndani?
7 Ndipo tsopano, Ambuye, ndilindira chiyani?
Chiyembekezo changa chili pa Inu.
8 Ndipulumutseni kwa zolakwa zanga zonse,
musandiike ndikhale chotonza cha wopusa.
9 Ndinakhala duu, sindinatsegule pakamwa panga;
chifukwa inu mudachichita.
10 Mundichotsere chovutitsa chanu;
pandithera ine chifukwa cha kulanga kwa dzanja lanu.
11 Pamene mulanga munthu ndi zomdzudzula chifukwa cha mphulupulu,
mukanganula kukongola kwake monga mumachita ndi njenjete.
Indedi, munthu aliyense ali chabe.
12 Imvani pemphero langa, Yehova,
ndipo tcherani khutu kulira kwanga;
musakhale chete pa misozi yanga;
Pakuti ine ndine mlendo ndi Inu,
wosakhazikika, monga makolo anga onse.
13 Ndiloleni, kuti nditsitsimuke,
ndisanamuke ndi kukhala kuli zii.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/39-1e42e71a4b9cc5abcfdee62c5502a571.mp3?version_id=1068—