Kuipitsitsa kwa anthu, kukometsetsa kwa Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova.
1 Cholakwa cha woipayo chimati m’kati mwa mtima wanga,
palibe kuopa Mulungu pamaso pake.
2 Pakuti adzidyoletsa yekha m’kuona kwake,
kuti anthu sadzachipeza choipa chake ndi kukwiya nacho.
3 Mau a pakamwa pake ndiwo opanda pake ndi onyenga,
waleka kuzindikira ndi kuchita bwino.
4 Alingirira zopanda pake pakama pake;
adziika panjira posati pabwino;
choipa saipidwa nacho.
5 Yehova, m’mwamba muli chifundo chanu;
choonadi chanu chifikira kuthambo.
6 Chilungamo chanu chikunga mapiri a Mulungu;
maweruzo anu akunga chozama chachikulu,
Yehova, musunga munthu ndi nyama.
7 Ha! Chifundo chanu, Mulungu, nchokondedwadi!
Ndipo ana a anthu athawira kumthunzi wa mapiko anu.
8 Adzakhuta kwambiri ndi zonona za m’nyumba mwanu,
ndipo mudzawamwetsa mu mtsinje wa zokondweretsa zanu.
9 Pakuti chitsime cha moyo chili ndi Inu,
M’kuunika kwanu tidzaona kuunika.
10 Tanimphitsani chifundo chanu pa iwo akudziwa Inu;
ndi chilungamo chanu pa oongoka mtima.
11 Phazi la akudzikuza lisandifikire ine,
ndi dzanja la oipa lisandichotse.
12 Pomwepo padagwera ochita zopanda pake.
Anawalikha, ndipo sadzatha kuukanso.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/36-41066793019d717dbea4c3065b406512.mp3?version_id=1068—