Categories
MASALIMO

MASALIMO 33

Alemekeza Mulungu wolenga, wosunga zonse

1 Fuulani mokondwera mwa Yehova, inu olungama mtima,

oongoka mtima ayenera kulemekeza.

2 Yamikani Yehova ndi zeze;

muimbireni ndi chisakasa cha zingwe khumi.

3 Mumuimbire Iye nyimbo yatsopano;

muimbe mwaluso kumveketsa mau.

4 Pakuti mau a Yehova ali olunjika;

ndi ntchito zake zonse zikhulupirika.

5 Iye ndiye wakukonda chilungamo ndi chiweruzo,

dziko lapansi ladzala ndi chifundo cha Yehova.

6 Zakumwamba zinalengedwa ndi mau a Yehova;

ndipo ndi mpweya wa m’kamwa mwake khamu lao lonse.

7 Amaunjika madzi a m’nyanja monga mulu,

amakundika zakudya mosungiramo.

8 Dziko lonse lapansi liope Yehova,

ponse pali anthu achite mantha chifukwa cha Iye.

9 Pakuti ananena, ndipo chinachitidwa;

analamulira, ndipo chinakhazikika.

10 Yehova aphwanya upo waamitundu,

asandutsa chabe zolingirira za mitundu ya anthu.

11 Chiweruzo cha Yehova chikhazikika chikhazikikire,

zolingirira za m’mtima mwake ku mibadwomibadwo.

12 Wodalitsika mtundu wa anthu

umene Yehova ndiye Mulungu wao;

mtundu womwe anausankha ukhale cholowa cha Iye yekha.

13 Yehova apenyerera m’mwamba;

aona ana onse a anthu.

14 M’malo akhalamo Iye, amapenya pansi

pa onse akukhala m’dziko lapansi.

15 Iye amene akonza mitima ya iwo onse,

amene azindikira zochita zao zonse.

16 Palibe mfumu yoti gulu lalikulu limpulumutsa,

mphamvu yaikulu siichilanditsa chiphona.

17 Kavalo safikana kupulumuka naye,

chinkana mphamvu yake njaikulu sapulumutsa.

18 Taonani, diso la Yehova lili pa iwo akumuopa Iye,

pa iwo akuyembekeza chifundo chake.

19 Kupulumutsa moyo wao kwa imfa,

ndi kuwasunga ndi moyo m’nyengo ya njala.

20 Moyo wathu walindira Yehova;

Iye ndiye thandizo lathu ndi chikopa chathu.

21 Pakuti mtima wathu udzakondwera mwa Iye,

chifukwa takhulupirira dzina lake loyera.

22 Yehova, chifundo chanu chikhale pa ife,

monga takuyembekezani Inu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/33-290a5e48f820310e3fb6c329165e9f93.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *