Davide popempha Mulungu amweruze, atchula zokoma zake
Salimo la Davide.
1 Mundiweruze, Yehova, pakuti ndayenda mu ungwiro wanga,
ndipo ndakhulupirira Yehova, sindadzaterereka.
2 Mundiyesere, Yehova, ndipo mundisunthe;
yeretsani impso zanga ndi mtima wanga.
3 Pakuti chifundo chanu chili pamaso panga;
ndipo ndayenda m’choona chanu.
4 Sindinakhala pansi ndi anthu achabe;
kapena kutsagana nao anthu othyasika.
5 Ndidana nao msonkhano wa ochimwa,
ndipo sindidzakhala nao pansi ochita zoipa.
6 Ndidzasamba manja anga mosalakwa;
kuti ndizungulire guwa la nsembe lanu, Yehova;
7 kuti ndimveketse mau a chiyamiko,
ndi kulalikira ntchito zanu zonse zozizwa.
8 Yehova, ndikonda chikhalidwe cha nyumba yanu,
ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.
9 Musandichotsere mzimu wanga pamodzi ndi olakwa,
kapena moyo wanga pamodzi ndi anthu okhetsa mwazi;
10 amene m’manja mwao muli mphulupulu,
ndi dzanja lao lamanja ladzala ndi zokometsera mlandu.
11 Koma ine, ndidzayenda mu ungwiro wanga;
mundiombole, ndipo ndichitireni chifundo.
12 Phazi langa liponda pachidikha,
m’misonkhano ndidzalemekeza Yehova.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/26-98dd20ba10f08be410bb9361a3194952.mp3?version_id=1068—