Categories
MASALIMO

MASALIMO 26

Davide popempha Mulungu amweruze, atchula zokoma zake

Salimo la Davide.

1 Mundiweruze, Yehova, pakuti ndayenda mu ungwiro wanga,

ndipo ndakhulupirira Yehova, sindadzaterereka.

2 Mundiyesere, Yehova, ndipo mundisunthe;

yeretsani impso zanga ndi mtima wanga.

3 Pakuti chifundo chanu chili pamaso panga;

ndipo ndayenda m’choona chanu.

4 Sindinakhala pansi ndi anthu achabe;

kapena kutsagana nao anthu othyasika.

5 Ndidana nao msonkhano wa ochimwa,

ndipo sindidzakhala nao pansi ochita zoipa.

6 Ndidzasamba manja anga mosalakwa;

kuti ndizungulire guwa la nsembe lanu, Yehova;

7 kuti ndimveketse mau a chiyamiko,

ndi kulalikira ntchito zanu zonse zozizwa.

8 Yehova, ndikonda chikhalidwe cha nyumba yanu,

ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.

9 Musandichotsere mzimu wanga pamodzi ndi olakwa,

kapena moyo wanga pamodzi ndi anthu okhetsa mwazi;

10 amene m’manja mwao muli mphulupulu,

ndi dzanja lao lamanja ladzala ndi zokometsera mlandu.

11 Koma ine, ndidzayenda mu ungwiro wanga;

mundiombole, ndipo ndichitireni chifundo.

12 Phazi langa liponda pachidikha,

m’misonkhano ndidzalemekeza Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/26-98dd20ba10f08be410bb9361a3194952.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *