Categories
MASALIMO

MASALIMO 24

Ulemerero wa Yehova

Salimo la Davide.

1 Dziko lapansi nla Yehova ndi zodzala zake zomwe,

dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhala m’mwemo.

2 Pakuti Iye analimanga pazinyanja,

nalikhazika pamadzi.

3 Adzakwera ndani m’phiri la Yehova?

Nadzaima m’malo ake oyera ndani?

4 Woyera m’manja, ndi woona m’mtima, ndiye;

iye amene sanakweze moyo wake kutsata zachabe,

ndipo salumbira monyenga.

5 Iye adzalandira dalitso kwa Yehova,

ndi chilungamo kwa Mulungu wa chipulumutso chake.

6 Uwu ndi mbadwo wa iwo akufuna Iye,

iwo akufuna nkhope yanu, Mulungu wa Yakobo.

7 Weramutsani mitu yanu, zipata inu;

ndipo kwezekani inu, zitseko zosatha,

kuti Mfumu ya ulemerero ilowe.

8 Mfumu imene ya ulemerero ndani?

Yehova wamphamvu ndi wolimba,

Yehova wolimba kunkhondo.

9 Weramutsani mitu yanu, zipata inu;

inde weramutsani, zitseko zosatha inu,

kuti Mfumu ya ulemerero ilowe.

10 Mfumu imene ya ulemerero ndani?

Yehova wa makamumakamu,

ndiye Mfumu ya ulemerero.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/24-0f47e0f7343c5bc9f37210a8a529040a.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *