Ulemerero wa Yehova
Salimo la Davide.
1 Dziko lapansi nla Yehova ndi zodzala zake zomwe,
dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhala m’mwemo.
2 Pakuti Iye analimanga pazinyanja,
nalikhazika pamadzi.
3 Adzakwera ndani m’phiri la Yehova?
Nadzaima m’malo ake oyera ndani?
4 Woyera m’manja, ndi woona m’mtima, ndiye;
iye amene sanakweze moyo wake kutsata zachabe,
ndipo salumbira monyenga.
5 Iye adzalandira dalitso kwa Yehova,
ndi chilungamo kwa Mulungu wa chipulumutso chake.
6 Uwu ndi mbadwo wa iwo akufuna Iye,
iwo akufuna nkhope yanu, Mulungu wa Yakobo.
7 Weramutsani mitu yanu, zipata inu;
ndipo kwezekani inu, zitseko zosatha,
kuti Mfumu ya ulemerero ilowe.
8 Mfumu imene ya ulemerero ndani?
Yehova wamphamvu ndi wolimba,
Yehova wolimba kunkhondo.
9 Weramutsani mitu yanu, zipata inu;
inde weramutsani, zitseko zosatha inu,
kuti Mfumu ya ulemerero ilowe.
10 Mfumu imene ya ulemerero ndani?
Yehova wa makamumakamu,
ndiye Mfumu ya ulemerero.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/24-0f47e0f7343c5bc9f37210a8a529040a.mp3?version_id=1068—