Categories
MASALIMO

MASALIMO 21

Davide ayamika Mulungu pa kugonjetsa adani

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Yehova, adzasekera mfumu mu mphamvu yanu;

adzakondwera kwakukulu m’chipulumutso chanu!

2 Mwampatsa iye chikhumbo cha mtima wake,

ndipo simunakane pempho la milomo yake.

3 Pakuti mufika kwa iye ndi madalitso okoma;

muika korona wa golide woyengetsa pamutu pake.

4 Anakupemphani moyo, mwampatsa iye;

mwamtalikitsira masiku kunthawi za nthawi.

5 Ulemerero wake ngwaukulu mwa chipulumutso chanu;

mumchitira iye ulemu ndi ukulu.

6 Pakuti mumuikira madalitso kunthawi zonse;

mumkondweretsa ndi chimwemwe pankhope panu.

7 Pakuti mfumu akhulupirira Yehova,

ndipo mwa chifundo cha Wam’mwambamwamba sadzagwedezeka iye.

8 Dzanja lanu lidzapeza adani anu onse,

dzanja lanu lamanja lidzapeza iwo akuda Inu.

9 Mudzawaika ngati ng’anjo yamoto pa nyengo ya mkwiyo wanu.

Yehova adzawatha m’kukwiya kwake,

ndipo moto udzawanyeketsa.

10 Mudzaziononga zobala zao kuzichotsa padziko lapansi,

ndi mbeu zao mwa ana a anthu.

11 Pakuti anakupangirani choipa,

anapangana chiwembu, osakhoza kuchichita.

12 Pakuti mudzawabweza m’mbuyo,

popiringidza m’nsinga zanu pankhope pao.

13 Kwezekani, Yehova, mu mphamvu yanu;

potero tidzaimba ndi kulemekeza chilimbiko chanu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/21-3b1823598324ec263045853364f077b7.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *