Kupempherera mfumu potulukira iye kunkhondo
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.
1 Yehova akuvomereze tsiku la nsautso;
dzina la Mulungu wa Yakobo likuike pamsanje;
2 likutumizire thandizo lotuluka m’malo oyera,
ndipo likugwirizize kuchokera muZiyoni;
3 likumbukire zopereka zako zonse,
lilandire nsembe yako yopsereza;
4 likupatse cha mtima wako,
ndipo likwaniritse upo wako wonse.
5 Tidzafuula mokondwera mwa chipulumutso chanu,
ndipo m’dzina la Mulungu wathu tidzakweza mbendera;
Yehova akwaniritse mapempho ako onse.
6 Tsopano ndidziwa kuti Yehova apulumutsa wodzozedwa wake;
adzamvomereza mu Mwamba mwake moyera
ndi mphamvu ya chipulumutso cha dzanja lake lamanja.
7 Ena atama magaleta, ndi ena akavalo;
koma ife tidzatchula dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 Iwowa anagonjeka, nagwa;
koma ife tauka, ndipo takhala chilili.
9 Yehova, pulumutsani,
mfumuyo ativomereze tsiku lakuitana ife.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/20-17416fa199165412977454d9dde10c18.mp3?version_id=1068—