Ufumu wa wodzozedwa wa Yehova
1 Aphokoseranjiamitundu,
nalingiriranji anthu zopanda pake?
2 Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi,
nachita upo akulu pamodzi,
Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, ndi kuti,
3 Tidule zomangira zao,
titaye nsinga zao.
4 Wokhala m’mwambayo adzaseka;
Ambuye adzawanyoza.
5 Pomwepo adzalankhula nao mu mkwiyo wake,
nadzawaopsa mu ukali wake.
6 Koma Ine ndadzoza mfumu yanga
PaZiyoni, phiri langa loyera.
7 Ndidzauza za chitsimikizo:
Yehova ananena ndi Ine,
Iwe ndiwe Mwana wanga; Ine lero ndakubala.
8 Undifunse, ndipo ndidzakupatsa amitundu
akhale cholowa chako,
ndi malekezero a dziko lapansi akhale akoako.
9 Udzawathyola ndi ndodo yachitsulo;
udzawaphwanya monga mbiya ya woumba.
10 Tsono, mafumu inu, chitani mwanzeru;
langikani, oweruza inu a dziko lapansi.
11 Tumikirani Yehova ndi mantha,
ndipo kondwerani ndi chinthenthe.
12 Mpsompsoneni Mwanayo, kuti angakwiye,
ndipo mungatayike m’njira
ukayaka pang’ono pokha mkwiyo wake.
Odala onse akumkhulupirira Iye.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/2-0cb4e5951d6c2f03d6a79956f669cf45.mp3?version_id=1068—