Categories
MASALIMO

MASALIMO 16

Munthu wokhulupirira Mulungu akhazikika mtima, osaopa kutayika

Mikitamu wa Davide.

1 Ndisungeni ine, Mulungu: pakuti ndakhulupirira Inu.

2 Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Ambuye wanga,

ndilibe chabwino china choposa Inu.

3 Za oyera mtima okhala padziko lapansi,

iwo ndiwo omveka mbiri,

mwa iwowo muli chikondwero changa chonse.

4 Zidzachuluka zisoni zao za iwo otsata Mulungu wina.

Sindidzathira nsembe zao zamwazi,

ndipo sindidzatchula maina ao pakamwa panga.

5 Yehova ndiye gawo la cholowa changa ndi chikho changa,

ndinu wondigwirira cholandira changa.

6 Zingwe zandigwera mondikondweretsa;

inde cholowa chokoma ndili nacho.

7 Ndidzadalitsa Yehova, amene anandichitira uphungu,

usikunso impso zanga zindilangiza.

8 Ndaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse;

popeza ali padzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.

9 Chifukwa chake wasekera mtima wanga,

nukondwera ulemu wanga;

mnofu wanganso udzakhala mokhazikika.

10 Pakuti simudzasiya moyo wanga kumanda;

simudzalola wokondedwa wanu avunde.

11 Mudzandidziwitsa njira ya moyo,

pankhope panu pali chimwemwe chokwanira;

m’dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/16-f9ecd68e0862fca5c3c92330c486c3b5.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *