Munthu wokhulupirira Mulungu akhazikika mtima, osaopa kutayika
Mikitamu wa Davide.
1 Ndisungeni ine, Mulungu: pakuti ndakhulupirira Inu.
2 Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Ambuye wanga,
ndilibe chabwino china choposa Inu.
3 Za oyera mtima okhala padziko lapansi,
iwo ndiwo omveka mbiri,
mwa iwowo muli chikondwero changa chonse.
4 Zidzachuluka zisoni zao za iwo otsata Mulungu wina.
Sindidzathira nsembe zao zamwazi,
ndipo sindidzatchula maina ao pakamwa panga.
5 Yehova ndiye gawo la cholowa changa ndi chikho changa,
ndinu wondigwirira cholandira changa.
6 Zingwe zandigwera mondikondweretsa;
inde cholowa chokoma ndili nacho.
7 Ndidzadalitsa Yehova, amene anandichitira uphungu,
usikunso impso zanga zindilangiza.
8 Ndaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse;
popeza ali padzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
9 Chifukwa chake wasekera mtima wanga,
nukondwera ulemu wanga;
mnofu wanganso udzakhala mokhazikika.
10 Pakuti simudzasiya moyo wanga kumanda;
simudzalola wokondedwa wanu avunde.
11 Mudzandidziwitsa njira ya moyo,
pankhope panu pali chimwemwe chokwanira;
m’dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/16-f9ecd68e0862fca5c3c92330c486c3b5.mp3?version_id=1068—