Chikhalidwe cha munthu woona wa Mulungu
Salimo la Davide.
1 Yehova, ndani adzagonera m’chihema mwanu?
Adzagonera ndani m’phiri lanu lopatulika?
2 Iye wakuyendayo mokwanira, nachita chilungamo,
nanena zoonadi mumtima mwake.
3 Amene sasinjirira ndi lilime lake,
nachitira mnzake choipa,
ndipo satola miseche pa mnansi wake.
4 M’maso mwake munthu woonongeka anyozeka;
koma awachitira ulemu akuopa Yehova.
Atalumbira kwa tsoka lake, sasintha ai.
5 Ndalama zake sakongoletsa mofuna phindu lalikulu,
ndipo salandira chokometsera mlandu kutsutsa wosachimwa.
Munthu wakuchita izi sadzagwedezeka kunthawi zonse.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/15-b5acfb14ce5ab7bfc019521093f17172.mp3?version_id=1068—