Categories
MASALIMO

MASALIMO 147

Alemekeze dzina la Mulungu chifukwa cha zokoma amachitira anthu ake

1 Aleluya; Pakuti kuimbira zomlemekeza Mulungu wathu nkokoma;

pakuti chikondweretsa ichi, chilemekezo chiyenera.

2 Yehova amangaYerusalemu;

asokolotsa otayika a Israele.

3 Achiritsa osweka mtima,

namanga mabala ao.

4 Awerenga nyenyezi momwe zili;

azitcha maina zonsezi.

5 Ambuye wathu ndi wamkulu ndi wa mphamvu zambiri;

nzeru yake njosatha.

6 Yehova agwiriziza ofatsa;

atsitsira oipa pansi.

7 Yamikani Yehova ndi kuthira mang’ombe;

muimbireni Mulungu wathu zomlemekeza pazeze:

8 Amene aphimba thambo ndi mitambo,

amene akonzera mvula nthaka,

amene aphukitsa msipu pamapiri.

9 Amene apatsa zoweta chakudya chao,

ana a khwangwala alikulira.

10 Mphamvu ya kavalo siimkonda:

Sakondwera nayo miyendo ya munthu.

11 Yehova akondwera nao akumuopa Iye,

iwo akuyembekeza chifundo chake.

12 Yerusalemu, lemekezani Yehova;

Ziyoni, lemekezani Mulungu wanu.

13 Popeza analimbitsa mipiringidzo ya zitseko zanu:

Anadalitsa ana anu m’kati mwanu.

14 Ndiye amene akhalitsa malire anu mumtendere;

akukhutitsani ndi tirigu wakucha bwino.

15 Atumiza lamulo lake kudziko lapansi;

mau ake athamanga liwiro.

16 Apatsa chipale chofewa ngati ubweya;

awaza chisanu ngati phulusa.

17 Aponya matalala ake ngati zidutsu:

Adzaima ndani pa kuzizira kwake?

18 Atumiza mau ake nazisungunula;

aombetsa mphepo yake, ayenda madzi ake.

19 Aonetsa mau ake kwa Yakobo;

malemba ake, ndi maweruzo ake kwa Israele.

20 Sanatero nao anthu a mtundu wina;

ndipo za maweruzo ake, sanawadziwe.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/147-908d9874eb731e84402030f8fb68f978.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *