Categories
MASALIMO

MASALIMO 146

Chifooko cha munthu, chikhulupiriko cha Mulungu

1 Aleluya;

Ulemekeze Yehova, moyo wanga.

2 Ndidzalemekeza Yehova m’moyo mwanga;

ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wanga pokhala ndi moyo ine.

3 Musamakhulupirira zinduna,

kapena mwana wa munthu, amene mulibe chipulumutso mwa iye.

4 Mpweya wake uchoka, abwerera kunka kunthaka yake;

tsiku lomwelo zotsimikiza mtima zake zitayika.

5 Wodala munthu amene akhala naye

Mulungu wa Yakobo kuti amthandize,

chiyembekezo chake chili pa Yehova, Mulungu wake.

6 Amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi,

nyanja ndi zonse zili m’mwemo.

Ndiye wakusunga choonadi kosatha,

7 ndiye wakuchitira chiweruzo osautsika;

ndiye wakupatsa anjala chakudya;

Yehova amasula akaidi.

8 Yehova apenyetsa osaona;

Yehova aongoletsa onse owerama;

Yehova akonda olungama.

9 Yehova asunga alendo;

agwiriziza mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye;

koma akhotetsa njira ya oipa.

10 Yehova adzachita ufumu kosatha,

Mulungu wako,Ziyoni, ku mibadwomibadwo.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/146-682faa55b24b87d18539b47852aa329c.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *