Chifooko cha munthu, chikhulupiriko cha Mulungu
1 Aleluya;
Ulemekeze Yehova, moyo wanga.
2 Ndidzalemekeza Yehova m’moyo mwanga;
ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wanga pokhala ndi moyo ine.
3 Musamakhulupirira zinduna,
kapena mwana wa munthu, amene mulibe chipulumutso mwa iye.
4 Mpweya wake uchoka, abwerera kunka kunthaka yake;
tsiku lomwelo zotsimikiza mtima zake zitayika.
5 Wodala munthu amene akhala naye
Mulungu wa Yakobo kuti amthandize,
chiyembekezo chake chili pa Yehova, Mulungu wake.
6 Amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi,
nyanja ndi zonse zili m’mwemo.
Ndiye wakusunga choonadi kosatha,
7 ndiye wakuchitira chiweruzo osautsika;
ndiye wakupatsa anjala chakudya;
Yehova amasula akaidi.
8 Yehova apenyetsa osaona;
Yehova aongoletsa onse owerama;
Yehova akonda olungama.
9 Yehova asunga alendo;
agwiriziza mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye;
koma akhotetsa njira ya oipa.
10 Yehova adzachita ufumu kosatha,
Mulungu wako,Ziyoni, ku mibadwomibadwo.
Aleluya.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/146-682faa55b24b87d18539b47852aa329c.mp3?version_id=1068—