Davide apempha Mulungu amlanditse msanga kwa adani ake
Salimo la Davide.
1 Imvani pemphero langa, Yehova; nditcherere khutu kupemba kwanga;
ndiyankheni mwa chikhulupiriko chanu, mwa chilungamo chanu.
2 Ndipo musaitane mlandu wa mtumiki wanu;
pakuti pamaso panu sipadzakhala wolungama wamoyo mmodzi yense.
3 Pakuti mdani alondola moyo wanga;
apondereza pansi moyo wanga;
andikhalitsa mumdima monga iwo adafa kale lomwe.
4 Potero mzimu wanga wakomoka mwa ine;
mtima wanga utenga nkhawa m’kati mwanga.
5 Ndikumbukira masiku a kale lomwe;
zija mudazichita ndilingirirapo;
ndikamba pandekha za ntchito ya manja anu.
6 Nditambalitsira manja anga kwa Inu:
Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.
7 Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha.
Musandibisire nkhope yanu;
ndingafanane nao akutsikira kudzenje.
8 Mundimvetse chifundo chanu mamawa;
popeza ndikhulupirira Inu:
Mundidziwitse njira ndiyendemo;
popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.
9 Mundilanditse kwa adani anga, Yehova;
ndibisala mwa Inu.
10 Mundiphunzitse chokonda Inu; popeza Inu ndinu Mulungu wanga;
Mzimu wanu ndi wokoma; munditsogolere kuchidikha.
11 Mundipatse moyo, Yehova, chifukwa cha dzina lanu;
mwa chilungamo chanu mutulutse moyo wanga m’sautso.
12 Ndipo mwa chifundo chanu mundidulire adani anga,
ndipo muononge onse akusautsa moyo wanga;
pakuti ine ndine mtumiki wanu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/143-c4534d5452662442eac4ab35bfdad210.mp3?version_id=1068—