Pemphero pakuopsedwa kwakukulu
Chilangizo cha Davide, muja anakhala m’phanga; Pemphero.
1 Ndifuula nalo liu langa kwa Yehova;
ndi mau anga ndipemba kwa Yehova.
2 Nditsanulira kudandaula kwanga pamaso pake;
ndionetsa msauko wanga pamaso pake.
3 Pamene mzimu wanga unakomoka m’kati mwanga, munadziwa njira yanga.
M’njira ndiyendamo ananditchera msampha.
4 Penyani kudzanja lamanja ndipo muone; palibe wondidziwa;
pothawirapo pandisowa; palibe mmodzi wosamalira moyo wanga.
5 Ndinafuulira kwa inu, Yehova;
ndinati, Inu ndinu pothawirapo panga,
gawo langa m’dziko la amoyo.
6 Tamverani kufuula kwanga; popeza ndisauka kwambiri;
ndilanditseni kwa iwo akundilondola; popeza andipambana.
7 Tulutsani moyo wanga m’ndende, kuti ndiyamike dzina lanu;
olungama adzandizinga;
pakuti mudzandichitira zokoma.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/142-4d4719bacbb778eb570fed3078acd2bf.mp3?version_id=1068—