Categories
MASALIMO

MASALIMO 142

Pemphero pakuopsedwa kwakukulu

Chilangizo cha Davide, muja anakhala m’phanga; Pemphero.

1 Ndifuula nalo liu langa kwa Yehova;

ndi mau anga ndipemba kwa Yehova.

2 Nditsanulira kudandaula kwanga pamaso pake;

ndionetsa msauko wanga pamaso pake.

3 Pamene mzimu wanga unakomoka m’kati mwanga, munadziwa njira yanga.

M’njira ndiyendamo ananditchera msampha.

4 Penyani kudzanja lamanja ndipo muone; palibe wondidziwa;

pothawirapo pandisowa; palibe mmodzi wosamalira moyo wanga.

5 Ndinafuulira kwa inu, Yehova;

ndinati, Inu ndinu pothawirapo panga,

gawo langa m’dziko la amoyo.

6 Tamverani kufuula kwanga; popeza ndisauka kwambiri;

ndilanditseni kwa iwo akundilondola; popeza andipambana.

7 Tulutsani moyo wanga m’ndende, kuti ndiyamike dzina lanu;

olungama adzandizinga;

pakuti mudzandichitira zokoma.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/142-4d4719bacbb778eb570fed3078acd2bf.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *